FB IMG 1746245883909

Phungu wa dera la pakati pa boma la Mangochi wa chipani cha Democratic Progressive (DPP) Victoria Kingstone wati sapikana nawo pa chisankho cha chipulula chomwe chipanichi chikuyembezereka kuchititsa mawa pa 3 May.

A Kingstone ati mwa ichi azapikisana nawo ngati phungu wa nyumba ya malamulo pa chisankho chapa 16 September ngati phungu oima payenkha koma izi sizikutanthauza kuti atuluka chipani cha DPP.

Izi zikudza pamene pali mphekesera kuti kuderali, chiwerengero cha nthumwi zomwe zikuyenera kusankha yemwe adzaimire chipanichi ngati phungu chaonjezeleka kusiyana ndi chikonzero cha komiti ya chipanichi m’derali.

“Adindo atitsekera chitseko, olo kuti tipange nawo chisankho ndaona kuti sichikhala cha bata ndi mtendere nde ine ndachiona cha nzeru kusapanga nawo komabe ndine membala wa DPP”. Atero a Kingstone.

Kudera lomweli, anthu enanso asanu ndi mmodzi 6 a chipani cha DPP omwe amafuna kudzayimira nawo pa udindo wa khansala ati sapikisana nawo pa chisankho cha chipululachi.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  ACB recommends prosecution for irregular recruitment of Phalombe hospital staff

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *