Friday, December 1Malawi's top news source
Shadow

Akonza Mapemphero Othana Ndi Ziwanda Mdziko

Wolemba: Rachael Julaye, LILONGWE

Kukula kwa mchitidwe ophana mwa chisawawa, umbava komanso ziwawa mdziko muno kwapangitsa gulu la abusa la Pastors Link komanso mzika zokhudzidwa kukonza mapemphero ofuna kuthana ndi ziwanda zomwe akuti zikukolezera zonsezi.

Mneneri wa omwe akonza mwambowu, Evangelist Stevie Chimwaza wati mapempherowa achitikira ku Robins Park Hall munzinda wa Blantyre Lolemba sabata ya mawa.

Chimwaza wati akufuna kubwera pa maso pa Mulungu pa zinthu zambiri zomwe zikupitilira kubala chisoni chochuluka pakati pa aMalawi.

Apa, iye wapempha aMalawi akufuna kwabwino kuti abwere mwaunyinji kudzakhala nawo pa mwambowu.

”Ndipemphe aMalawi asataye mtima kaamba koti Mulungu amamva komanso amayankha. Tili ndi chiyembekezo kuti mapempherowa tichita m’mizinda yonse ya mdziko muno.

“Koma pakadali pano, tipemphe anzathu a nyumba zoulutsa mawu kuti atithandize kuulutsa mwambowu kuti anthu onse athe kutenga nawo mbali,” watero Chimwaza.

Mapempherowa akudza kutsatira imfa zomwe zakhala zikuchitika mdziko muno maka ku Lilongwe komwe anthu anayi anaphedwa msabata imodzi.

Kuonjezera apo, mchitidwe wa umbanda ndi umbava wafika povuta kwambiri mdziko muno zomwe akatswiri ena olankhula pa zosiyanasiyana akuti zitha kugwirizana kwambiri ndi kusokonekera kwa chuma mdziko muno.

Masiku angapo apitawo, nduna yofalitsa nkhani Moses Kunkuyu idauza aMalawi kuti boma lichita chilichonse pofuna kuonetsetsa kuti chitetezo chili mchimake kuti anthu adzichita ntchito zawo mwa ufulu.

Iwo adatinso awonetsetsa kuti kafukufuku pa imfa za anthu omwe aphedwa masiku apitawa achitike bwino kuti aMalawi adziwe chilungamo.

Koma kumayambiliro, nduna ya za chitetezo, Ken Zikhale Ng’oma idakwiyitsa aMalawi komanso magulu omenyera ufulu pomwe idati kuphedwa kwa anthu atatu okha pa anthu 20 million sizikusonyeza kuti mdziko muno mulibe chitetezo.

Giving you more news Malawi Freedom Network News

NEEF Customers Demands Their Deposit Back

A group of business people who applied for National Economic Empowerment Fund (Neef) loans in Mzuzu tstormed office premises for Read more

Police move to protect persons with albinism

Malawi Police Service has engaged traditional healers in Mwanza on how to protect persons with albinism in the district. Speaking Read more

MARTHA CHIZUMA DECLARES WAR AGAINST CHAKWERA: SAYS PRESIDENT, JUDICIARY, ARMY AND POLICE CORRUPT

In a shocking tale to absorb, ACB boss Martha Chizuma has taken her corruption fight against her bosses, openly going Read more

Police in Chitipa district have arrested Kayange who poured hot water on her husband

According to Chitipa Police PRO Gladwell Simwaka, on March 7, 2022 the victim Blair Kuyokwa, 35, returned home in the Read more

Lilongwe Police recover stolen items

Police in Lilongwe have for the second time this month recovered household items and other property worth over 23 million Read more

Police at Bangwe in Blantyre have arrested three suspects

*Police at Bangwe in Blantyre have arrested three suspects and recovered some items they allegedly stole at Namiyango Assemblies of Read more

CSO SPEAKS AGAINST Anti-Ashok Nair Demos: Says they are ‘Criminal’ in Nature

The Citizen Advancement for Economic Revolution has described the anti-Ashok Nair demonstrations scheduled for tomorrow Wednesday as criminal in nature. Read more

M’tengo wa pakete imodzi ya shuga, tsopano ukumafanana ndi wa bread m’modzi

Izi zadza chifukwa bread wakwela mtengo kufika pa 1 000 Kwacha m'modzi , m'magolosale ena. Akuluakulu ena omwe ali ndi Read more

Police Summon Gaffar Over Death Threats

Details have emerged indicating that Malawi Police has summoned Rafik Gaffar of R Gaffar Transport for series of death threats Read more

Wife Follows Husband To Prison For Permitting Defilement Of Her Daughter

A 36-year old mother Maimuna Kassim who hails from Mikundi Village in the area of Traditional Authority Mponda, in Mangochi Read more

News To Read

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *