Friday, December 1Malawi's top news source
Shadow

Atoht Manje wadzudzula khalidwe la nsanje mu nyimbo yake ya ‘Nchape’

Oimbayu, yemwe amadziwika bwino ndi nyimbo zokhudza umoyo komanso chikhalidwe cha anthu, walandira chiyamiko pa nyimbo yake yatsopano yomwe akuitcha, “Nchape.”

Mu nyimboyi, Elias Missi, yemwe amadziwika bwino ndi dzina loti Atoht Manje, wayankhula motsutsana ndi mchitidwe wa nsanje omwe akuti ndi oononga.

Mkuluyu, yemwe mu kanema wa nyimboyi wagwilitsa ntchito anthu ovina chamba cha Beni, akudzudzula anthu omwe amapanga zinthu za ena.

Atoht Manje akuyimba kunena kuti, “Mphuno zawo zili bize kufwenkha… kufwenkha bizinezi zayeni, kufwenkha zomwe wawadalitsa mulungu,” apa oimbayu akungotsindika za momwe anthu akhalidwe amazipelekera akafuna kuchita za ena.

Iye akupitilira kunena kuti anthuwa ali ndi miyendo ya mphamvu yomwe imakhala ndi kuthekela kofika kulikonse komwe angakachite mjedo, kukambirana nkhani zokhudza anzawo.

“Miyendo yawo siitopa kuyenda, yakaliyakali anzanga kuyendako, kusaka ojeda nawo… kujeda nyengo za anzawo…” watero Atoht Manje.

Mu nyimboyi, Atoht Manje akuti anthu akhalidwe lotere akudwala ndipo akufunika mankhwala, ndipo mankhwalawa akutchula kuti “Nchape”.

Kuno ku Malawi, “Nchape” umadziwika ndi mbiri yotsuka mthupi.

Ndi chifukwa chake iye akuti anthuwa akuyenela kupatsidwa “Nchape,” kuti achile ku nthenda ya mjendo.

Izi zili mu kolasi ya nyimboyi momwe akuti, “Apatseni Nchape..Akumva kuwawa…Mwina Nchape uchotse nsanje mumtimamo… adziwe moyo simpikisano…”

Ngakhale nyimboyi ili ya chamba chachiMalawi (lokolo), zaonetsa kuti ili ndi chikoka kutengera ndi ndemanga zomwe zayankhulidwa pa nyimboyi.

Mwachidule, Atoht Manje mu nyimboyi akudzudzula khalidwe la mijedo lomwe akuti ndi loipa, lomwe malinga ndi iye, lakhazikika mmitima ya anthu mdziko muno.

Giving you more news Malawi Freedom Network News

Brian Banda Returns To Times TV

Brian Banda has returned to times TV after he was unceremoniously fired at State House He was live On Times Read more

Gambling, Betting Is An Entertainment Not Source Of Income

Malawi Gaming and National Lotteries Board, has urged Malawians to start viewing gambling and betting as an entertainment and not Read more

Govt And Private Sector Inspired To Invest In Local Film Industry

In the picture; Skinnebach speaking during one of the events The government and private sector are being inspired to invest Read more

Multi award winning Christian pop rock ‘The Afters and The Grove Band’ is set hold nation wide shows.

According to organisers of the shows 'Live Love', the band will start their performances in Lilongwe on 18th June at Read more

South African Dancer Zodwa Wabantu Stopped Not Perform In Malawi

The Ministry of Tourism, Culture and Wildlife has stopped a show scheduled for Dominic's in Blantyre on June 11 2022 Read more

No To Nakedness In Public -Minister

A South African dancer Zodwa Wabantu, real name Rebecca Libram who was poised to perform at Dominic’s Hotel in Blantyre Read more

FDH Bank Plc has pumped in K15 million to Sand Music Festival.

The banks Marketing and Communications Manager Lorraine Chikhula says the move is part of its corporate social responsibility. Representative of Read more

MBC TV2 Engages Corporate World

After interacting with content creators earlier in the day, Malawi Broadcasting Corporation management engaged the corporate world in Lilongwe. MBC Read more

MBC To Launch MBC TV2

Malawi Broadcasting Cooperation will this year launch the MBC TV 2. While disclosing that all is set for the launch Read more

BLANTYRE 42 .195 KILOMETRE RACE ON

Organisers of this year's Blantyre City Marathon say the 42.195 kilometres race is this Sunday 4 September 2022. The competition Read more

News To Read

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *