Malamulo akumulola Chilima -UTM

Chipani cha UTM chatsutsa malipoti akuti wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino yemweso ndi mtsogoleri wa chipanichi,Saulos Chilima sali woyenera kudzapikisana nawo pa mpando wa utsogoleri wa dziko pa chisankho cha chaka cha m’mawa.

Izi zikudza pomwe anthu ambiri pa masamba a m’chezo akhala akuyankhula kuti Chilima sali woyenera kudzaimira nawo pa mpando wa utsogoleri wa dziko lino malingana ndi malamulo.

Koma m’neneri wa chipanichi, Felix Njawala wawuza Timveni Online kuti malamulo akumulola Chilima ngakhale wakhala wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino kwa materemu awiri.

Njawala wati pali anthu ena omwe akufalitsa nkhanizi mwadala ndi cholinga chongofuna kusokoneza komanso kuchotsa chidwi cha a Malawi pa a Chilima.

See also  Biased Mainstream Malawi Media jealously overrating Martha Chizuma while criminating Zuneth Sattar

Leave a Reply

Your email address will not be published.Required fields are marked *