
Dekhani, Ndikukumbukira Malonjezo Anga-Katsonga
Anthu m’dera la Zalewa m’boma la Neno ati akupitilira kusautsika ndi vuto lakusowa kwa madzi aukhondo pomwe phungu wa kunyumba ya malamulo kumwera kwa bomali, Mark Katsonga Phiri wati akukumbukira za malonjezo omwe adapereka koma wapempha anthuwa kuti adekhe.
AKatsonga, omwenso ndi nduna yaza malonda ndi mafakitale, anena izi pa mkumano omwe anachititsa ndi mafumu komanso anthu akudera la Zalewa pomwe amawafunila mafuno abwino a chikondwerelo cha khilisimisi ndi chaka cha tsopano.
Iwo anati akukumbukira bwino kuti adalonjeza kubweretsa madzi a m’mipope komanso sukulu ya secondale pa Zalewa koma wati mliri wa Covid-19 ndi omwe wakhala ukupinga zina mwa ntchito za chitukukozi.
Apa, iye wapempha anthu akuderali kuti adekhe ponena kuti malonjezowa akwaniritsidwa posachedwa.
Ndipo ...