Kwavuta:Nkokenkoke Pa Nkhani Ya Buluma

FB IMG 1669215393328

Mlangizi wa boma pa nkhani za malamulo Thabo Chakaka Nyirenda wasemphana zochita ndi komiti ya Public Appointments-PAC pa nkhani yoti yemwe adali wachiwiri kwa mkulu wa NOCMA, mai Hellen Buluma akaonekere ku nyumbayi kuti akafotokoze mwatchutchutchu zomwe adalemba mu kalata yawo yosiya ntchito.

FB IMG 1669215399786

Mwa zina, a Buluma adati wapampando wa board ya NOCMA yemwenso ndi mlembi mu ofesi ya mtsogoleri wa dziko ndi nduna zake, mai Colleen Zamba, akuluakulu ena a chipani cha MCP komanso a boma ankawakakamiza kuti adzipereka ma contract mwachinyengo.

Koma a Chakaka Nyirenda auza Sipikala wa nyumba ya malamulo, Catherine Gotani Hara kuti a Buluma komanso a Zamba asawonekere ku komiti-yi pomwe PAC yati ipitilira ndi ganizo lake lofunsa awiriwa.

Kodi nkoyeneradi kuti mai Buluma ndi mai Zamba ayankhe mafunso?

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *