“`President Lazarus Chakwera wataya mlongo wawo Mirriam Chakwera yemwe wamwalira lero.
Mlembi wa atolankhani a President Anthony Kasunda walengeza za imfa ya mlongo wake wa Chakwera mwachidule.
A Kasunda adaonjeza kuti Chakwera wathetsa nthawi yomweyo zokambirana zake ndi anthu.
āMtsogoleri wa dziko lino ayambiranso zokambirana zake ndi anthu akayika maliro a mlongo wawo, zomwe zikuyenera kuchitika pa Epulo 20 māmudzi mwa Manase ku Mdika māboma la Dowa,ā adatero Kasunda.“`