IMG 20220503 WA0092

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) kumwera Kondwani Nankhumwa wanena mphekesera zoti akufuna kugulitsa chipanichi ku UTM kapena Malawi Congress Party (MCP).

A Nankhumwa amalankhula izi dzulo ku Lilongwe pa Mgona ground pomwe adachita msonkhano wa ndale.

Adayankha mphekesera zomwe zidamveka zoti akadzapambana kukhala Purezidenti wa DPP Nankhumwa alowa UTM kapena MCP.

Malinga ndi a Nankhumwa sangalowe UTM yomwe ili ndi aphungu anayi okha ku Nyumba ya Malamulo.

Adapitiliza kunena kuti iye ndi DPP ndipo sakuganiza zolowa chipani china chilichonse.

Malinga ndi a Nankhumwa ati adzapikisana nawo pa mpando wa utsogoleri kumsonkhanowu ndipo apambana ndi 95%.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *