Tony Ngalande

Phungu wa dera la kumpoto kwa boma la Balaka a Tony Ngalande wakhazikitsa ntchito yokonza misewu imene idaonongeka kumayambiliro a chaka chino kaamba ka namondwe wa Freddy, ngati njira imodzi yofuna kuonetsetsa kuti ntchito za malonda zikupitilira m’derali.

Poyankhula pamene amakhazikitsa ntchitoyi, a Ngalande adati iwo achita izi pofuna kuonetsetsa kuti anthu a madera osiyanasiyana kuzungulira bomali akhale ndi mayendedwe abwino, pofuna kupititsa patsogolo ntchito za malonda.

Pa mwambowu, phunguyu anaperekanso zofunda kwa anthu achikulire ndi ovutika okwana 200 komanso cheke cha ndalama zokwana K8 miliyoni ngati ngongole ku magulu a amayi komanso achinyamata.

Mayi Magret Msanama a zaka 76, a dera la Kandengwe ayamikira phunguyu kaamba ka thandizoli ponena kuti liwanthandiza kwambiri mu nyengo ino yozizira.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *