Malawi Freedom Network
Giving you daily news that rock the world
ExclusiveLocal

CCTV Lati Zionetsero Zokhudza Ngozi Ya Ndege Ya Ku Chikangawa Zikhalepo

Bungwe la Concerned Citizens Timely Voice (CCTV) laikira kumbuyo ganizo la bungwe la CDEDI lochita ziwonetsero pa nkhani yokhudza ngozi ya ndege ya ku Chikangawa.

Malingana ndi kalata yomwe bungweli latulutsa yati papita miyezi pafupifupi isanu ndi imodzi chichitikireni ngozi ya ndege-yi koma palibe cholozeka chomwe boma likunena zokhudza kukhazikitsa komiti ya padera kuti ifufuze za ngoziyi.

Bungweli lapempha anthu onse omwe akufuna kudziwa chilungamo pa imfa ya Dr Saulos Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu kuti adzatenge nawo gawo pa ziwonetserozi.

Bungwe la CDEDI motsogozedwa ndi mkulu wa bungweli a Sylvester Namiwa akonza ziwonetsero lachinayi likubwerali pofuna kukakamiza mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera kuti akhazikitse komiti ya padera kuti ifufuze bwino za ngoziyi ndikupeza mayankho a mafunso omwe aMalawi ali nawo okhudza ngoziyi.

Related posts

SPARC Systems committed to IT excellency, community development in Africa

Malawi Freedom Network

‘Cashgate’ returns under the Tonse Alliance Government

By Burnett Munthali

Controversy! Namibia to Cull Over 700 Wild Animals Amid Severe Drought

Malawi Freedom Network

Kamtukule faces controversy: Kaliati disowns Minister, analysts suggest political motives

Malawi Freedom Network

President Chakwera arrives in China for FOCAC summit

By Suleman Chitera

Airtel Malawi forecasts widened loss for 2023

Malawi Freedom Network

Leave a Comment

* By using this form you agree with the storage and handling of your data by this website.

Leave a review

This website uses cookies to improve your experience. We'll assume you're ok with this, but you can opt-out if you wish. Accept Read More