Download 2

CCTV Lati Zionetsero Zokhudza Ngozi Ya Ndege Ya Ku Chikangawa Zikhalepo

Bungwe la Concerned Citizens Timely Voice (CCTV) laikira kumbuyo ganizo la bungwe la CDEDI lochita ziwonetsero pa nkhani yokhudza ngozi ya ndege ya ku Chikangawa.

Malingana ndi kalata yomwe bungweli latulutsa yati papita miyezi pafupifupi isanu ndi imodzi chichitikireni ngozi ya ndege-yi koma palibe cholozeka chomwe boma likunena zokhudza kukhazikitsa komiti ya padera kuti ifufuze za ngoziyi.

Bungweli lapempha anthu onse omwe akufuna kudziwa chilungamo pa imfa ya Dr Saulos Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu kuti adzatenge nawo gawo pa ziwonetserozi.

Bungwe la CDEDI motsogozedwa ndi mkulu wa bungweli a Sylvester Namiwa akonza ziwonetsero lachinayi likubwerali pofuna kukakamiza mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera kuti akhazikitse komiti ya padera kuti ifufuze bwino za ngoziyi ndikupeza mayankho a mafunso omwe aMalawi ali nawo okhudza ngoziyi.

More From Author

FB IMG 1729396405158 300x152

titha Kutembenuza Tebulo

IMG 20241020 WA0030 300x146

Mirriam’s Triumphant Journey: From Near Marriage to Academic Excellence

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ella Brown

Project Manager

Darkness cannot drive out darkness; only light can do that. Hate cannot drive out hate: only love can do that.