download 2

Bungwe la Concerned Citizens Timely Voice (CCTV) laikira kumbuyo ganizo la bungwe la CDEDI lochita ziwonetsero pa nkhani yokhudza ngozi ya ndege ya ku Chikangawa.

Malingana ndi kalata yomwe bungweli latulutsa yati papita miyezi pafupifupi isanu ndi imodzi chichitikireni ngozi ya ndege-yi koma palibe cholozeka chomwe boma likunena zokhudza kukhazikitsa komiti ya padera kuti ifufuze za ngoziyi.

Bungweli lapempha anthu onse omwe akufuna kudziwa chilungamo pa imfa ya Dr Saulos Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu kuti adzatenge nawo gawo pa ziwonetserozi.

Bungwe la CDEDI motsogozedwa ndi mkulu wa bungweli a Sylvester Namiwa akonza ziwonetsero lachinayi likubwerali pofuna kukakamiza mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera kuti akhazikitse komiti ya padera kuti ifufuze bwino za ngoziyi ndikupeza mayankho a mafunso omwe aMalawi ali nawo okhudza ngoziyi.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *