TILI NDI CHIKHULUPILIRO KUTI AMENE TIKUWAFUNAWO ATULA PANSI UDINDO WAWO – ATERO MZIKA ZOKHUZIDWA ZOMWE ZINACHITA ZIWONETSERO LERO
M’modzi mwa anthu omwe amatsogolera ziwonetsero zomwe zachitika mu mzinda wa Blantyre pofuna kuti nduna ya za chitetezo cha m’dziko a Ken Zikhale Ng’oma komanso mkulu wa nthambi ya Immigration atule pansi udindo wati ali ndi chikhulupiliro kuti awiriwa achita monga iwo akufunira.
A Edward Kambanje ati ndunayi yalephera ntchito kotero ikungoyenera kuti itule pansi udindo.
Iwo ati nzomvetsa chisoni kuti nthambi yoona zolowa ndi kutuluka m’dziko muno idanamiza anthu kuti yayambiraso ntchito yopanga ziphaso pomwe mpaka pano anthu akuvutikabe kupeza ziphasozi.
Iwo ati ndunayi komanso mkulu wa nthambi ya Immigration a Charles Kalumo akungoyenera kuti atule pansi udindo kuti anthu ena abwere ndi kuyesako nzeru zina.
Gulu lina lomwe likudzitcha mzika zokhudzidwa zidachita zoonetserozi pofuna kuonetsa kusakondwa ndi zomwe zikuchitika ku nthambi yoona zolowa ndi kutuluka m’dziko muno.