FB IMG 1656370757250

Chilima Alankhula Ku Mtundu Wa Amalawi Lachisanu

Dr. Saulos Chilima ati Lachisanu likudzali alankhula ku mtundu wa Malawi ngati wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko komanso mtsogoleri wa UTM pa zinthu zomwe zikuchitika m’dziko lino zomwe ndizofunikira.

M’neneri wa UTM, Frank Mwenifumbo watsimikiza izi ndipo wati izi zidzachitikira ku ofesi ya chipanichi ku Area 10 munzinda wa Lilongwe.

Pakadalipano, a Chilima apempha otsatira chipanichi komanso a Malawi kuti adekhe.

Lachisanu lapitali, Dr..Chilima adati anthu asayese kupusa kufatsa komwe adaonetsa pomwe dziko lino linkakonzekera chisankho cha mtsogoleri wa dziko mu June 2020.

Dr. Chilima alankhulanso patangotha masiku ochepa atakana kotheratu kuti sakudziwapo kanthu pa kuwaganizira kuti adachita za katangale ndi Zuneth Sattar.

More From Author

IMG 20220627 WA0133 300x238

DPP Geared To Bounce Back- Chaponda

600x315 5 300x158

Apolisi a Malawi akuimbidwa mlandu wokakamiza a Mussa kuti anene zabodza

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ella Brown

Project Manager

Darkness cannot drive out darkness; only light can do that. Hate cannot drive out hate: only love can do that.