
“Tikuzunzika Tipatseni Malipiro Athu
Anthu ena ogwira ntchito ku bungwe la ADMARC adandaula kuti akuzunzika komanso kuponderezedwa kuchokera pomwe boma lidatseka bungweli kuti likonze zinthu.
Izi azinena pomwe anthu oposa 300 ogwira ntchito ku bungweli achita zionetsero m’mawawu pofuna kukamiza boma kuti liwapatse malipiro awo a mwezi wa September ndi October.
Iwo akufunanso boma lichite machawi pokonzanso zinthu ku bungweli.
Read also: Kamwendo Back To His Roots
Read also: Morocco Earn US$20.5 Million Despite World Cup Quarter-final Exit
Read also: Malawi Freedom Network Crowns Joseph Mwanamvekha “Minister of the Year” for Exceptional Leadership
Ambiri mwa omwe amachita zionetserozi anavala makaka akuda.
Anthu okwana 4687 akuyembekezeka kuchotsedwa ntchito ku ADMARC pomwe boma likuti likufuna kukonzanso ntchito za bungweli pomwe zikumveka kuti ogwira ntchito ena amasaka chuma.
Read also: Saudi Arabia Reaffirms Support for Malawi’s Economic Recovery and Development
Read also: Dowa CSO Network Assures Of Voicing Out Impunity
Read also: Government to implement Farmer Challenge Fund SAPP 11 project




















