Chipani cha MCP chati chikudziwa bwino kuti kuwonjezera madera a phungu komanso makhansala kufuna ndalama zochuluka komabe nkofunika mogwirizana ndi malamulo kuti ganizo la bungwe la MEC ligwire ntchito basi.
M’neneri wa chipanichi, Maurice Munthali wadzudzulanso chipani cha DPP ati posafuna kulemekeza malamulo m’mbuyomu ponena kuti zimapangitsa kuti anthu asamalandire zitukuko mofanana.
Read also: Malawians in solemn remembrance of SKC,and eight others
Read also: Castle Announce K16 Million Sponsorship To Sand Music Festival
Read also: Citizens for Credible Elections Granted Permission to Protest in Lilongwe
Posachedwapa, nyumba ya malamulo idavomereza lipoti la MEC lowonjezera madera a aphungu kuchoka pa 193 kufika pa 229 ndipo madera a makhansala afika pa 509 kuchoka pa 462.
Koma DPP yati kuwonjezera maderawa nkusaganiza kamba koti pakadalipano dziko lino likudutsa kale m’mavuto adzaoneni pachuma.
Read also: Put Interests Malawi First, Gwengwe
Read also: Malawi Manufacturers Choked by K4,000 Dollar Black Market
Read also: Kalindo expresses concern about Malawian deportees from South Africa





