Mivi iwiri yavulaza Mapale

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yalephera kufika mu ndime ina yampikisano wa CAF Champions League kutsatira kugonja 2-0 ndi timu ya Red Arrows pamasewero omwe analipo lero pa bwalo la National Heroes ku Lusaka m’dziko la Zambia.

Saddam Yusuf Phiri anapeza chigoli kudzera pa penote mu mphindi 65 ndipo Paul Katema anabwera ndi msomali omaliza kutangotsala mphindi zisanu kuti masewerowa athe.

Red Arrows Overcome Nyasa Big Bullets in Thrilling CAF Champions League Clash

Mapale amafunika chipambano pamasewero a lero potengera kuti amatsogola 2-1 pamasewero oyamba omwe anaseweredwa pa bwalo la Bingu mu nzinda wa Lilongwe.

Arrows yapita chitsogolo ndi zigoli zitatu kwa ziwiri kuphatikizira masewero onse ndipo adzakumana ndi TP Mazembe pamasewero otsatira amu mpikisanowu.

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Please disable your adblocker or whitelist this site!