Mneneri wachipani cha Democratic Progressive (DPP) Shadreck Namalomba wati ndiwodabwa kuti mtsogoleri wadziko lino akuwuza mtundu wa a Malawi kuti boma lake labweretsa mafuta agalimoto lachitatu kudzera panjanji.

Izi zikudza pomwe mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera lachitatu analandila sitima yapanjanji yobweletsa mafuta agalimoto m’boma la Nsanje yomwe akuti patha zaka zoposa 40 isanakuyenda.

Komatu malingana ndi a Namalomba izi sizoona ponena kuti njanjeyi yamanga ndi boma la Mozambique kuchoka ku Beira kufika pa malire adziko lino ndi dziko la Mozambique.

“Komasotu a Kongelesi akulephela kuwauza aMalawi chilungamo kuti zanjanjezi tidayambitsa ndife a DPP ndipo tidzazimalizitsaso tokha tikadzalowa m’boma 2025” atelo a Namalomba.

Mwazina a Namalomba ati zikanakhala bwino boma lidakamanena chilungamo chifukwa amalawi akudutsa kale mu nyengo zowawa.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *