Mneneri wachipani cha Democratic Progressive (DPP) Shadreck Namalomba wati ndiwodabwa kuti mtsogoleri wadziko lino akuwuza mtundu wa a Malawi kuti boma lake labweretsa mafuta agalimoto lachitatu kudzera panjanji.
Izi zikudza pomwe mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera lachitatu analandila sitima yapanjanji yobweletsa mafuta agalimoto m’boma la Nsanje yomwe akuti patha zaka zoposa 40 isanakuyenda.
Komatu malingana ndi a Namalomba izi sizoona ponena kuti njanjeyi yamanga ndi boma la Mozambique kuchoka ku Beira kufika pa malire adziko lino ndi dziko la Mozambique.
“Komasotu a Kongelesi akulephela kuwauza aMalawi chilungamo kuti zanjanjezi tidayambitsa ndife a DPP ndipo tidzazimalizitsaso tokha tikadzalowa m’boma 2025” atelo a Namalomba.
Mwazina a Namalomba ati zikanakhala bwino boma lidakamanena chilungamo chifukwa amalawi akudutsa kale mu nyengo zowawa.
MALAWI
FREEDOM
NETWORK
United for Freedom, Justice and a Better Malawi
Airtel Money
0994095804
Mpamba
0881428759
FDH Bank
Acc No:
1400000670385NBS Bank
Acc No:
10118988Thank you for your support!