Mtsogoleri wa chipani cha MCP Dr. Lazarus Chakwera wadzudzula omwe akumalowetsa imfa ya wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino wakale Dr. Saulos Chilima munkhani za ndale.

Iwo ati anthu atenge zomwe zidatuluka mulipoti la akatswiri am’dziko la Germany komanso madotolo a m’dziko muno zokhudza ngozi ya ndege yomwe idapha a Chilima ndi anthu ena 8.

Mtsogoleriyu wati iwo ndi a Chilima anagwilizana zopanga ndale zotukula miyoyo ya a Malawi osati ndale zopakana matope.

Iwo ati ndi mtsogoleri yemwe wachita zitukuko zosiyanasiyana m’dziko muno ndipo athokoza anthu achipanichi powapasanso mwayi oti apitilize kutsogolera chipanichi.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *