FB IMG 1749982490391

Mzika za m’maiko a dziko lino komanso Zambia zavulira chipewa mtsogoleri wakale wadziko lino Bakili Muluzi kaamba kothandizira kuthetsa kusamvana komwe kunalipo pakati paboma la dziko la Zambia komanso akubanja la mtsogoleri wakale wadzikolo Edgar Chagwa Lungu pankhani yokhudza maliro a mtsogoleriyu.

Kumwalira kwa a Lungu womwe adamwalira masiku apitawa kunadzetsa mpungwepungwe pakati pambali ziwilizi mdzikolo pomwe boma limaimba milandu chipani cha a Lungu pankhani zina kumeneko.

Panalinso ma lipoti onena kuti a Lungu adanenelatu kuti mtsogoleri wa dziko la Zambia Hakainde Hichilema asadzapezeke pa maliro a Lungu kutsatila kusamvana pandale komwe kwakhala kulipo kwa zaka zambiri pakati pa atsogoleri-wa.

Kusamvanaku kunafika pamponda
-chimela pomwe boma la dzikolo linalepheletsa mwambo otumiza thupi la a Lungu kuchoka mdziko la South Africa kupita ku Zambia pa 11 June malingana ndi chikonzero cha akubanja.

Komatu a Muluzi komanso anthu ena analowelerapo ndikuthandizira kuti ma kusemphana chichewa pankhaniyi kuthe ndipo pakadali pano mbali anthu ayamikila mtsogoleri wakale-yu.

Kumwalira kwa a Lungu kukutanthauza kuti dziko la Zambia lilibe mtsogoleri wakale yemwe ali moyo.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  MCP holds rally at Njewa Primary School with Chimwendo Banda

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *