Lekani Kunamiza Anthu Nthawi Yosankha” – Shepherd Bushiri

By Suleman Chitera

Mneneri Shepherd Bushiri, mtsogoleri wa mpingo wa The Jesus Nation Church, walangiza andale kuti asiye kunamiza a Malawi ndi malonjezano abodza pomwe dziko likukonzekera chisankho mu mwezi wa mawa.

Kudzera pa tsamba lake la Facebook, Bushiri wanena kuti andale ayenera kuyankhula zoona ndikulonjeza zinthu zomwe angakwanitse kuchita akasankhidwa, osati kubwereza mabodza.

“Lekani kuuza anthu zinthu zomwe inu simungakwanitse kuchita mutasankhidwa. Dziko lathuli lili m’mavuto aakulu ndipo likufunika mtsogoleri amene angatsogolere mwachilungamo komanso mwachikondi. Lonjezani zomwe mungakwanitse.” – Shepherd Bushiri

Ichi ndi koyamba kuti Bushiri, yemwenso ndi wochita malonda komanso ntchito zachifundo, ayankhule poyera zokhudza zisankho zomwe zikuchitika pa 16 September.

Share and Enjoy !

Shares

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Shares