FB IMG 1755008485984
Listen to this article

By Suleman Chitera

Mneneri Shepherd Bushiri, mtsogoleri wa mpingo wa The Jesus Nation Church, walangiza andale kuti asiye kunamiza a Malawi ndi malonjezano abodza pomwe dziko likukonzekera chisankho mu mwezi wa mawa.

Kudzera pa tsamba lake la Facebook, Bushiri wanena kuti andale ayenera kuyankhula zoona ndikulonjeza zinthu zomwe angakwanitse kuchita akasankhidwa, osati kubwereza mabodza.

“Lekani kuuza anthu zinthu zomwe inu simungakwanitse kuchita mutasankhidwa. Dziko lathuli lili m’mavuto aakulu ndipo likufunika mtsogoleri amene angatsogolere mwachilungamo komanso mwachikondi. Lonjezani zomwe mungakwanitse.” – Shepherd Bushiri

Ichi ndi koyamba kuti Bushiri, yemwenso ndi wochita malonda komanso ntchito zachifundo, ayankhule poyera zokhudza zisankho zomwe zikuchitika pa 16 September.

See also  Chakwera left fuming after being denied chance to speak at SKC Foundation launch

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *