FB IMG 1755008485984

By Suleman Chitera

Mneneri Shepherd Bushiri, mtsogoleri wa mpingo wa The Jesus Nation Church, walangiza andale kuti asiye kunamiza a Malawi ndi malonjezano abodza pomwe dziko likukonzekera chisankho mu mwezi wa mawa.

Kudzera pa tsamba lake la Facebook, Bushiri wanena kuti andale ayenera kuyankhula zoona ndikulonjeza zinthu zomwe angakwanitse kuchita akasankhidwa, osati kubwereza mabodza.

“Lekani kuuza anthu zinthu zomwe inu simungakwanitse kuchita mutasankhidwa. Dziko lathuli lili m’mavuto aakulu ndipo likufunika mtsogoleri amene angatsogolere mwachilungamo komanso mwachikondi. Lonjezani zomwe mungakwanitse.” – Shepherd Bushiri

Ichi ndi koyamba kuti Bushiri, yemwenso ndi wochita malonda komanso ntchito zachifundo, ayankhule poyera zokhudza zisankho zomwe zikuchitika pa 16 September.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  Fertilizer Price Surge in Malawi a “Disaster” for Farmers, Warns Farmers Union

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *