Tue. Apr 30th, 2024

YONECO iyendera anthu pa msasa wa anthu othawa madzi ku Mangochi

By Suleman Chitera Mar23,2022

Olemba: Issa Prince Chimwala

Bungwe la Youthnet and Counseling (YONECO) lachiwiri linayendera anthu omwe akukhala pamsasa wa anthu othawa madzi osefukira kwa Chapola mdera la mfumu yaikulu Chimwala ku Mangochi. Pa Ulendowu, a Grant Dulla anapempha anthuwa pa msasawu kuti adzikondana komanso kukhulupirika kwa okondedwa awo.


“Nthawi ngati ino pamafunika kukondana pakati pa wina ndi nzake, mzanu ngati wachoka ndipo mwana wake anatsala ndipo akulira, msamaleni. Kwa anthu apabanja tikupempha kuti pakhale kukhulupirika. Sibwino kupita kunja mkumakapanga zibwezi chifukwa mapeto ake tidzatenganso matenda. Ife ngati bungwe la YONECO tidzibwera pamsasa pano kuonetsetsa kuti mukuthandizidwa moyenera”. Anatsiriza choncho.


Pa ulendowu, a Dulla analinso ndi Issa Chimwala yemwe ndi ophunzitsa anthu zinthu zosiyanasiyana kuchokera ku bungwe la NICE. Mkuyankhula kwawo a Issa Chimwala, anapempha adindo oyang’anira ngozi zogwa mwa dzidzidzi mderali kuti awasamalire anthuwa momwe angathere komanso anapempha anthu akufuna kwabwino kuti abwere adzathandize anthuwa pa mavuto omwe akukumana nawo.


M’modzi mwa a komiti ya Ngozi zogwa mwadzidzidzi a Rajab Hassan anathokoza mabungwe a YONECO ndi NICE kamba kodzacheza ndi anthuwa, iwo anati izi ziwalimbitsa mtima. Anthuwa anathokozanso a Komiti pamsasawu kamba ka chikondi ndi chisamaliro chomwe akuwapatsa.
Pamsasawu pali mabanja 70 omwe nyumba zawo zinagwa kamba ka mvula yamphamvu.

Related Posts

DPP Blues Rebels Brings Division In

DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open