Bungwe la CDEDI Malawi lalamula kuti mtsogoleri wadziko lino Lazarus Chakwera atsitse mtengo wafeteleza yemwe ali pansi pa zipangizo za ulimi zotsika mtengo.
Mkulu wa bungwe la CDEDI Sylvester Namiwa amalankhula ndi atolankhani lachinayi mumzinda wa Lilongwe.
Malingana ndi Namiwa, a Chakwera akuyenera kutsitsa mtengo wafetelezayu kuchoka pa MK15 000 kufika pa MK7500 pathumba asanakhazikitse ndondomeko yogulira zipangizo za ulimi zotsika mtengo pa 21 November.
Read also: ActionAid Strengthens Early Childhood Development in Balaka
Read also: Kamlepo Kalua tells Mec conduct credible elections
Read also: Malawi partners with ACMI on carbon credit
Mtsogoleri wabungwe la CDEDI-yu wachenjezanso boma kuti lisagulitse feteleza amene dziko la Malawi lalandira ngati thandizo kuchokera ku maiko ena, ndipo mmalo mwake agawe wa ulele kwa a Malawi.
A Namiwa alamulanso boma kuti litsekule misika yonse ya Admarc ndicholinga chakuti a Malawi asavutike kugula zipangizo za ulimi zotsika mtengo chaka chino.
Read also: Chakwera engages Lubeck University on fight against non NCDs
Read also: Critical questions surround plane crash investigation: Public demands clarity
Read also: Activist Agape Khombe Calls for Broad-Based Inquiry into Chilima Plane Crash





