Awa ndi mawu ochokera ku bungwe la Chewa Heritage Foundation (Chefo) lomwe layankhulapo pankhani yomwe ati inachitika kudera lina ku Monkey Bay m’boma la Mangochi kumene anamvetsedwa kuti gule wamkulu anamenya munthu mpaka kumwalira.
Poyankhulapo pa msonkhano wa atolankhani mu mzinda wa Lilongwe, mkulu woona za mafumu, magule ndi miyambo ku bungweli a Lyson Banda ati uyu sadali gule wamkulu koma munthu woyesezera guleyu pofuna kupezapo mwayi ochita zoipa.
Read also: Lawyer Alexius Kamangila Calls for Action on Corruption in the Judiciary
Read also: Concerned citizen fears for Malawi not to be a peaceful country
Read also: Aisha Adams Resigns as Chair of UDF Forthcoming Convention Amid Party Turmoil
A Banda anaonjezeranso kuti gule wamkulu samatuluka chisawawa komanso samayenera kuyenda atanyamula zida zoopsa monga zikwanje komanso nkhwangwa.
M’mawu ake mfumu yaikulu Masumbankhunda yapempha adindo kuti agwiritse ntchito malamulo pomanga yemwe wachita izi ponena kuti asayipitse chikhalidwe chawo.
Read also: Chakwera Accept Failure And Step Down.
Read also: Inquiry Findings Faults Martha Chizuma
Read also: Member of Parliament distributes maize flour to 200 households





