Awa ndi mawu ochokera ku bungwe la Chewa Heritage Foundation (Chefo) lomwe layankhulapo pankhani yomwe ati inachitika kudera lina ku Monkey Bay m’boma la Mangochi kumene anamvetsedwa kuti gule wamkulu anamenya munthu mpaka kumwalira.
Poyankhulapo pa msonkhano wa atolankhani mu mzinda wa Lilongwe, mkulu woona za mafumu, magule ndi miyambo ku bungweli a Lyson Banda ati uyu sadali gule wamkulu koma munthu woyesezera guleyu pofuna kupezapo mwayi ochita zoipa.
Read also: Analysis of the importance of Martyrs’ Day in Malawi
Read also: Smartmatic: Controversy, legal battles, and the future of election technology
A Banda anaonjezeranso kuti gule wamkulu samatuluka chisawawa komanso samayenera kuyenda atanyamula zida zoopsa monga zikwanje komanso nkhwangwa.
M’mawu ake mfumu yaikulu Masumbankhunda yapempha adindo kuti agwiritse ntchito malamulo pomanga yemwe wachita izi ponena kuti asayipitse chikhalidwe chawo.
Read also: Traffic Police : Things To Remember
Read also: Analysis: A contrast of leadership styles at the 79th UNGA
Read also: Pastor Shumba calls MDF to defend Malawians not MCP





