Awa ndi mawu ochokera ku bungwe la Chewa Heritage Foundation (Chefo) lomwe layankhulapo pankhani yomwe ati inachitika kudera lina ku Monkey Bay m’boma la Mangochi kumene anamvetsedwa kuti gule wamkulu anamenya munthu mpaka kumwalira.
Poyankhulapo pa msonkhano wa atolankhani mu mzinda wa Lilongwe, mkulu woona za mafumu, magule ndi miyambo ku bungweli a Lyson Banda ati uyu sadali gule wamkulu koma munthu woyesezera guleyu pofuna kupezapo mwayi ochita zoipa.
A Banda anaonjezeranso kuti gule wamkulu samatuluka chisawawa komanso samayenera kuyenda atanyamula zida zoopsa monga zikwanje komanso nkhwangwa.
M’mawu ake mfumu yaikulu Masumbankhunda yapempha adindo kuti agwiritse ntchito malamulo pomanga yemwe wachita izi ponena kuti asayipitse chikhalidwe chawo.
MALAWI
FREEDOM
NETWORK
United for Freedom, Justice and a Better Malawi
Airtel Money
0994095804
Mpamba
0881428759
FDH Bank
Acc No:
1400000670385NBS Bank
Acc No:
10118988Thank you for your support!