FB IMG 1748455555038

Awa ndi mawu ochokera ku bungwe la Chewa Heritage Foundation (Chefo) lomwe layankhulapo pankhani yomwe ati inachitika kudera lina ku Monkey Bay m’boma la Mangochi kumene anamvetsedwa kuti gule wamkulu anamenya munthu mpaka kumwalira.

Poyankhulapo pa msonkhano wa atolankhani mu mzinda wa Lilongwe, mkulu woona za mafumu, magule ndi miyambo ku bungweli a Lyson Banda ati uyu sadali gule wamkulu koma munthu woyesezera guleyu pofuna kupezapo mwayi ochita zoipa.

A Banda anaonjezeranso kuti gule wamkulu samatuluka chisawawa komanso samayenera kuyenda atanyamula zida zoopsa monga zikwanje komanso nkhwangwa.

M’mawu ake mfumu yaikulu Masumbankhunda yapempha adindo kuti agwiritse ntchito malamulo pomanga yemwe wachita izi ponena kuti asayipitse chikhalidwe chawo.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  UDF Deputy Leader Rahim Elias questions Police presence and inaction at protest site

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *