Sun. Apr 28th, 2024

Atatu ali mmanja mwa apolisi kamba kopha munthu

Anthu atatu anjatidwa kamba kowaganizila kuti apha a Charles Assan azaka 32 omwe amagwira ku Bank ya First Capita Bank m’boma la Dowa.

Mneneri wa Polisi ku Mponera a Macpatson Msadala ati atatuwa ndi a Jafali Mtungwe emwe ndi dalaivala wa Bungwe la NEEF , Nelson Jossam ndi chibwenzi chake Halima Kamwana.

Nkhaniyi ikuti Malemuwa ndi anthu ena awiri a Nelson Jossam ndi a Halima Kamwana atamaliza kumwa mowa pa Malo ena a Sunrise anakonza zomapita kwawo koma sanapeze Taxi iliyonse yoti iwatenge.

Ali mofufuzabe Taxi-yi iwo anaona Galimoto ina ya Toyota Hilux Pickup yomwe inali ya bungwe la NEEF ndipo imaendetsedwa ndi a Jafali Mtungwe ndipo atapepha anawaloledza kuwatenga kuti akawasiye ku dera la Nkhamanga.

Ali mu Galimotoli anasephana maganizo zomwe zinapangitsa kuti dalaivalayi awatulusemo ndipo atatulukamo woyendetsayi anayendetsa Galimoto yomwe inagunda Malemuwa.

Chipatala Chamadisi Mission chapedza kuti a Assan amwalira kamba kovuladzidwa pogundidwa komanso thupi lawo lapezeka ndimabala olumidwa.

Related Posts

Mirece supports land reclamation bought by foreigners

Reverend Flywell Somanje…. this is the way to go A governance and human rights organization, the Millennium Information and Resource Read more

NBM Donates K100 Million Towards Forest Restoration

National Bank of Malawi has committed K100 million for preservation and restoration of 6 natural resources in the country by Read more

I am not a crook— Mulli

MAINTAINED THAT PROCEDURES WERE FOLLOWED—Mulli— Picture by Catherine Maulidi Businessperson and National Bus Services Chairperson Leston Mulli on Tuesday told Read more

Navicha appointed as a leader of opposition in parliament

Member of parliament for Thyolo Thava, Mary Thom Navicha has been recently appointed as a new leader of opposition following Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open