Sat. Apr 27th, 2024

Chakwera Akhazikisa Ndondomeko Ya Zipangizo Zaulimi Zotsika mtengo ya AIP

By Suleman Chitera Nov19,2022

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, ku m’mawaku akuyembekezeka kutsogolera mwambo otsegulira ndondomeko ya zipangizo zaulimi zotsika mtengo ya AIP m’boma la Dedza.

Chaka chino, ndondomeko-yi yakhudzika ndi mavuto angapo kuphatikizapo malipoti akubedwa kwa ndalama zokwana K30 billion ngakhale boma lidakana izi ponena kuti ndalama zomwe likudziwa ndi K750 million.

Padakali pano, thumba la feteleza m’dziko muno lafika pa K75,000 ndipo alimi omwe apindule ndi AIP akhale akugula thumba pa K15,000.

Koma nduna ya za ulimi, Sam Kawale, yatsimikizira aMalawi kuti feteleza yemwe boma lagula komanso yemwe ena apereka ngati thandizo ndi okwanira kuti pasakhale zosamwitsa zili zonse.

Boma lidaika K109.4 billion ku AIP chaka chino yogulira feteleza oti apindulire alimi 2.5 million.

Chiwerengerochi chidatsika kuchoka pa 3 million kaamba ka kugwa kwa ndalama ya Kwacha komanso kukwera mtengo kwa feteleza.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open