Sat. Apr 27th, 2024

“Chakwera Ayimanso Pa Chisankho Cha 2025”

Komiti yaikulu ya chipani cha Malawi Congress -MCP, yabwereza kuti yagwirizana pa chiganizo choti mtsogoleri wa chipani-chi, Lazarus Chakwera, yemwenso ndi mtsogoleri wa dziko lino, aimire-nso chipani-chi pa chisankho chamu 2025.

Mlembi wamkulu wa MCP, Eisenhower Mkaka, wanena izi ku maofesi a chipani-chi ku Lilongwe, pambuyo pa mkumano wa komiti-yo yomwe Chakwera anatenga nawo mbali.

Iye wati komiti-yi inagwirizana pa chiganizo-chi m’mbuyomu, ndipo pa mkumano wa Lachitatu mamembala a komiti-yi aitsimikiza-nso.

Komabe, Mkaka wati mamembala a MCP ofuna mpando wa mtsogoleri wa chipani-chi ndi oloredwa kuti akapikisane ndi Chakwera ku msonkhano waukulu, omwe dongosolo lake alengeze mtsogolomu.

Malingana ndi malamulo a chipani cha MCP, munthu amayenera kukhala pa mpando wa mtsogoleri wa chipani-chi kwa zaka khumi, ndipo potengera izi pofija mu 2025 President Lazarus Chakwera akhala kuti wamaliza zaka khumi zokhala pa udindo-wu.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi business tycoon Simbi Phiri disassociates himself from forming up “Congress for Democrats”

Business Mogul Simbi Ashan Phiri who is Executive Chairman of Katho Civils has disassociated himself from social media rumours that Read more

Navicha appointed as a leader of opposition in parliament

Member of parliament for Thyolo Thava, Mary Thom Navicha has been recently appointed as a new leader of opposition following Read more

Govt Refutes Speculations Spreading On Social Media On Sattar Contracts

Minister of Information and Digitisation Moses Kunkuyu has justified the government’s decision to initiate a $19 million (about K32.3 billion) Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open