Thu. Apr 25th, 2024

Dekhani, Ndikukumbukira Malonjezo Anga-Katsonga

Anthu m’dera la Zalewa m’boma la Neno ati akupitilira kusautsika ndi vuto lakusowa kwa madzi aukhondo pomwe phungu wa kunyumba ya malamulo kumwera kwa bomali, Mark Katsonga Phiri wati akukumbukira za malonjezo omwe adapereka koma wapempha anthuwa kuti adekhe.

AKatsonga, omwenso ndi nduna yaza malonda ndi mafakitale, anena izi pa mkumano omwe anachititsa ndi mafumu komanso anthu akudera la Zalewa pomwe amawafunila mafuno abwino a chikondwerelo cha khilisimisi ndi chaka cha tsopano.

Iwo anati akukumbukira bwino kuti adalonjeza kubweretsa madzi a m’mipope komanso sukulu ya secondale pa Zalewa koma wati mliri wa Covid-19 ndi omwe wakhala ukupinga zina mwa ntchito za chitukukozi.

Apa, iye wapempha anthu akuderali kuti adekhe ponena kuti malonjezowa akwaniritsidwa posachedwa.

Ndipo poyankhapo pa nkhani ya kuchedwa kwa zipangizo za ulimi zotsika mtengo zomwe anthu kuderali anadandaula kuti sanayambe kugula, phunguyu wati achita chothekera kuti feteleza afikile m’madera ambiri kuti anthu adzipeza zipangizozi mosavuta.

M’mawu ake, Group Village Headman Zalewa inayamikila phunguyu kaamba kobwera kudzacheza ndi anthu kuderali koma anati ayang’anila kuti malonjezowa akwaniritsidwe mwachangu ponena kuti anthu akuderali akusautsika pa nkhani ya madzi aukhondo ndi maphunziro a secondale kaamba koti derali lilibe sukulu ya secondale ndi imodzi yomwe.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open