Thu. Apr 25th, 2024

DZAKA 12 CHIFUKWA CHOPEZEKA NDI NDALAMA ZA FAKE

By Suleman Chitera Apr25,2022

Bwalo la Magistrate ku Dwangwa m’boma la Nkhotakota lalamura kuti a Yesaya Quoto a dzaka zakubadwa 24, akakhale ku ndende ndi kugwira ntchito ya kalavula kwa dzaka 12, kamba kopezeka ndi ndalama zama k5000 a pepala za chinyengo zokwana k575, 000.

Quoto anamangidwa pa 28 March, 2022 pa Dwangwa Trading Center atapezeka ndi ndalamazi pomwe ankafuna kutumiza pa airtel Money kwa mayi wina pamalopo.

Agent wa airtel money-yu atazidabwa ndalamazo zomwe zimakwana k60, 000, adayitana anzake, ndipo adaganiza zodziwitsa apolisi apa Nkhunga police station omwe anabwera nkuzamanga oganiziridwayu.

Apolisi atamusecha anamupezanso ndi ndalama zina za chinyengo zokwana k115, 000 zokhala ndi serial number ya AA7915614.

Apolisi anapitanso kunyumba kwake kukalanda machine omwe akukhulupilira kuti ankagwiritsa ntchito popanga ndalamazi.

Apolisi anamutsegulira Quoto milandu itatu; opezeka ndi ndalama za chinyengo popanda chilolezo, opezeka ndi machine opangira ndalama za chinyengo, komanso opanga ndalama za chinyengo.

Bwalo la milandu linapeleka dzaka 4 ku mlandu oyamba, dzaka zina 4 ku mlandu wachiwiri, komanso dzaka 12 ku mlandu wachitatu. Zilango zonsezi zigwira ntchito nthawi imodzi.

Yesaya Quoto amachokera m’mudzi mwa Mwerekete, T/A Mthwalo, m’boma la Mzimba.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open