Monday, March 27Malawi's top news source
Shadow

DZAKA 12 CHIFUKWA CHOPEZEKA NDI NDALAMA ZA FAKE

Bwalo la Magistrate ku Dwangwa m’boma la Nkhotakota lalamura kuti a Yesaya Quoto a dzaka zakubadwa 24, akakhale ku ndende ndi kugwira ntchito ya kalavula kwa dzaka 12, kamba kopezeka ndi ndalama zama k5000 a pepala za chinyengo zokwana k575, 000.

Quoto anamangidwa pa 28 March, 2022 pa Dwangwa Trading Center atapezeka ndi ndalamazi pomwe ankafuna kutumiza pa airtel Money kwa mayi wina pamalopo.

Agent wa airtel money-yu atazidabwa ndalamazo zomwe zimakwana k60, 000, adayitana anzake, ndipo adaganiza zodziwitsa apolisi apa Nkhunga police station omwe anabwera nkuzamanga oganiziridwayu.

Apolisi atamusecha anamupezanso ndi ndalama zina za chinyengo zokwana k115, 000 zokhala ndi serial number ya AA7915614.

Apolisi anapitanso kunyumba kwake kukalanda machine omwe akukhulupilira kuti ankagwiritsa ntchito popanga ndalamazi.

Apolisi anamutsegulira Quoto milandu itatu; opezeka ndi ndalama za chinyengo popanda chilolezo, opezeka ndi machine opangira ndalama za chinyengo, komanso opanga ndalama za chinyengo.

Bwalo la milandu linapeleka dzaka 4 ku mlandu oyamba, dzaka zina 4 ku mlandu wachiwiri, komanso dzaka 12 ku mlandu wachitatu. Zilango zonsezi zigwira ntchito nthawi imodzi.

Yesaya Quoto amachokera m’mudzi mwa Mwerekete, T/A Mthwalo, m’boma la Mzimba.

Related News
NEEF Customers Demands Their Deposit Back

A group of business people who applied for National Economic Empowerment Fund (Neef) loans in Mzuzu tstormed office premises for Read more

Dipak Jevant Paid for None Supplied Fertiliser

Dipak Jevant Paid for None Supplied Fertiliser

OPC, CMS Violates Access To Information Law.

The Office of the President and Cabinet - OPC and the Central Medical Stores Trust, have become the first public Read more

Mponela Police Arrest Isaac Levison For Possessing Indian Hemp

Police in Mponela have arrested 23 year old Isaac Levison, for being found in possession of 8 pails of Indian Read more

Kapichira Rehabilitation Work Start Next month

There are now hopes for improved power outages in Malawi as power generator EGENCO has disclosed plans to commence reconstruction Read more

10 Suspected Traffickers In Police Custody

2 police officers at Area 30 arrested too With the recent surge in Trafficking in Persons cases, Police reveal they Read more

Neno Joins Battle Against Dc Transfers

Some residents of Neno District including chiefs have risen against the announced transfer of their District Commissioner, Justin Kathumba, who Read more

Police Apologises UNIMA Students

In picture, Dokera receives the written apology from Eastern Region Deputy Commissioner of Police, Kelvin Mlezo WE WILL NOT DO Read more

Malawi Govt Scammed K30 Billion, Tonse Alliance Involved In A Syndicate

MINISTRY OF AGRICULTURE EXPOSES ITSELF NOW In what seems to be a defence for the SCAMMED 30 BILLION allegations that Read more

Buluma Summoned To Appear Before Court

The Chief Resident Magistrate's Court in Lilongwe has summoned National Oil Company of Malawi (Nocma) deputy chief executive officer (CEO) Read more

News To Read

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *