M’tengo wa pakete imodzi ya shuga, tsopano ukumafanana ndi wa bread m’modzi

Izi zadza chifukwa bread wakwela mtengo kufika pa 1 000 Kwacha m’modzi , m’magolosale ena.

Akuluakulu ena omwe ali ndi ma bakery, akuti mtengo wa tiligu, wakwela padziko lonse, zomwe zachititsanso kukwela kwa mtengo wa ufa opangila bread.

“Chomcho , ufa wopangila bread wachoka pa 36, 000 Kwacha kufika pa 48, 000 Kwacha , thumba limodzi la 50 kilograms,” watelo m’modzi mwa iwo.

Ndipo m’kulu wa bungwe la ogula malonda la Consumers Association of Malawi – CAMA, a John Kapito, wati boma lichitepo kanthu pa nkhani ya mitengoyi, chifukwa anthu m’dziko lino, avutika.
“`

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *