Ogwilizira mpando wa mtsogoleri wa bungwe la Super League of Malawi(Sulom), Colonel Gilbert Mitawa ayimira pa mpando wa mtsogoleri wa bungweri opanda opikitsana nawo.
Izi zikutsatira chikalata chomwe atulutsa a Crowe Howarth Malawi omwe amayendetsa ndondomeko yolandila ma kalata a anthu ofuna kuzayimila pa maudindo ku bungwe la Sulom omwe anatseka kulandila ma kalatawa.
A Mitawa omwe amagwilizira udindo’wu kutsatira kwa kuchoka kwa Fleetwood Haiya amene pano ndi mtsogoleri wa bungwe la Football Association of Malawi akuyembekezeka kupitiliza ngodya zomwe anasiya a Haiya zofuna kusintha mpira.
Pa udindo wa mamembala a komiti yayikulu ya bungweri pali anthu atatu omwe akupikisana omwe ali Isaac Mdindo, William Nhlane ndi Charles Manyungwa.
Zisankho zizachitika pa 30 March, 2024 mu mzinda wa Lilongwe.