Sat. Apr 27th, 2024

Sindikupanga Nawo Za Ndale, Ndine Mtumiki Wa Mulungu–Bushiri

M’neneri Shepherd Bushiri wati alibe malingaliro ofuna kuyamba ndale kapena kupikisana nawo pa chisankho cha mtsogoleri wa dziko chaka cha mawa.

A Bushiri, omwe ndi mtsogoleri wa mpingo wa ECG-The Jesus Nation ati iwo ndi mtumiki wa Mulungu amene cholinga chawo chakhazikika pogwira ntchito ndi boma lolamula ndipo adzapitiriza kutero.

Yemwe amawayankhulira, Aubrey Kusakala wati a Bushiri ndi wokhudzidwa ndi zimene anthu maka m’masamba a mchezo akhala akufalitsa kuti adzapikisana nawo pa chisankho cha mtsogoleri wa dziko.

A Kusakala apempha anthu amene akufalitsa izi kuti asiye kutero.
Pakadalipano, a Bushiri akuzungulira m’maboma a mdziko lino kugawa chimanga kwa anthu omwe akhudzidwa ndi njala yomwe yayala mphasa.

Iwo adati akufuna kufikira anthu okwana 1 million ndi thandizoli.

Related Posts
Paramount Holdings Donates Medical Equipments To Area 25 Health Centre

Paramount Holdings Limited has handed over medical equipment worth 3 million Kwacha to Area 25 health centre. The organisation's Operations Read more

I am not a crook— Mulli

MAINTAINED THAT PROCEDURES WERE FOLLOWED—Mulli— Picture by Catherine Maulidi Businessperson and National Bus Services Chairperson Leston Mulli on Tuesday told Read more

Navicha appointed as a leader of opposition in parliament

Member of parliament for Thyolo Thava, Mary Thom Navicha has been recently appointed as a new leader of opposition following Read more

Jumah says it is possible to change Malawi in 10-15 years

By Vincent Gunde President and Commander in Chief of Muvi wa Chilungamo Revolutionary Party (MRP) Bantu Saunders Jumah, says it Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open