Mbilizi ndi anzake atuluka pa belo

Bwalo la magistrate ku Blantyre latulutsa pa belo yemwe anali wachiwiri kwa komishonala wa bungwe lotolela msonkho la MRA a Roza Mbilizi ndi anzawo ena awiri

Anthuwa anawamanga kaamba kowaganizira kuti adagwiritsa ntchito molakwika nambala yopelekera msonkho (TPIN) ya mtsogoleli wakale wa dziko lino a Peter Mutharika.

Bwaloli lalamula atatuwa kuti alipile K 350,000 ngati chikole komanso kuti apeleke ku bwaloli zikalata zawo zoyendera komanso anthuwa auzidwa kuti azikaonekera ku mafesi a ACB pa sabata ziwiri zili zonse

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *