“Mlembi wamkulu mu ofesi ya mtsogoleri wa dziko lino Colleen Zamba, amakakamiza bungwe la NOCMA kuti lichite chinyengo pogula mafuta.”

Izi zaululika lero pomwe yemwe anali ogwirizira udindo wa mkulu wa bungwe la NOCMA, Hellen Buluma, anakaonekera ku komiti ya nyumba yamalamulo yowona zakalembedwe ka ntchito ka anthu m’boma.

Buluma anati amakakamizidwa ndi Zamba kuti apereke mwai obweretsa mafuta mdziko muno kwa munthu wina wa dziko la Nigeria yemwe amangodziwika kuti Chief komanso munthu wina yemwe akuti ndi Evarista Kamwangala, yemwe akukhala ku South Africa.

Ngati wapampando wa bungwe la NOCMA, Zamba amayenera kuonekera ku komitiyi masanawa pamodzi ndi amnzake koma sanafike ndipo sanapereke chifukwa chilichonse.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *