FB IMG 1679687679504

Kutsatira mvula yochuluka imene inadza kamba ka Namondwe wa Freddy, nyanja ya Chilwa ku Zomba yadzadza pomwe madzi tsopano afika midzi yoyandikana ndi nyanjayi.

Malingana ndi a Fanuel Sadik, amene amakhala kuderali, madzi afika midzi yoyandikila doko la Kachulu komanso Mchenga ndipo anthu asamukira madera ena.

Khansala waderali, a Douglas January, anatsimikiza izi ndipo anati pakali pano kufika kunyanjaku pagalimoto ndikosatheka.

Zithuzi zikuonetsa momwe zinthu ziliri ku nyanjayi.

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *