Khansara wa MCP a Gabriel Mwaungulu atula pansi udindo wawo

Khansala wa chipani cha Malawi Congress Party (MCP) wa Ward ya Chibavi East a Gabriel Mwaungulu atula pansi udindo wawo ndipo walowa chipani cha Alliance for Democracy (AFORD).

Mwaungulu adalengeza kusiya ntchito yake Lamulungu pa msonkhano wokumbukira zaka 30 womwe a Enoch Chihana adakonza pa Chibavi Ground mumzinda wa Mzuzu.

Khansala walonjeza kuti agwira ntchito molimbika pokopa anthu kuti avotere Chihana ndi AFORD pa chisankho chomwe chikubwera cha 2025.

Panopa bungwe la AFORD likuchita misonkhano m’dziko muno zisankho zisanachitike.

Chipanichi chikuyembekezeka kuchita msonkhano wawo wachisankho mu Seputembala

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Please disable your adblocker or whitelist this site!