Nduna yowona za chitetezo cha mdziko, Ken Zikhale Ng’oma yalandira mendulo ya ulemu kamba ka ntchito yomwe akugwira pogwira ndi kutumiza ku Rwanda anthu omwe akuganiziridwa kuti anapalamula milandu yokhuza nkhondo.
Malinga ndi Ng’oma, anthuwa akhala akufunidwa kuyambira mchaka cha 1994 ndipo boma likusaka anthu ena asanu kuti nawo atumizidwe ku Rwanda.
Malinga ndi Ng’oma, mphotoyi apereka ndi akulu akulu a dziko la Rwanda.
Dziko la Rwanda linalengeza kuti yemwe azapeze anthuwa azalandira chionamaso cha ndalama zokwana 2.5 million zamdziko la Amerika zomwe ndi pafupi fupi 2.5 billion kwacha.
Lachitatu lino anthu ena okwana makumi anayi akuyembekezeka kutumizidwanso ku Rwanda.
MALAWI
FREEDOM
NETWORK
United for Freedom, Justice and a Better Malawi
Airtel Money
0994095804
Mpamba
0881428759
FDH Bank
Acc No:
1400000670385NBS Bank
Acc No:
10118988Thank you for your support!