Thom Mpinganjira ndi wokondwa ndi wanderers

Mtsogoleri wa timu ya Mighty Mukuru Wanderers a Thom Mpinganjira wati ndi wokondwa ndi m’mene timuyi ikuchitira pa masewero ake a mu ligi ya TNM.

A Mpinganjira ati apempha osewera a timuyi kuti adzipereke kwatunthu pa masewero omwe atsala nawo kuti apitilire kupereka mpikisano wa ukulu ku timu ya Silver Strikers yomwe ikutsogola pakadali pano.

Iwo ayamikiranso osewera wa pakati wa timuyi Isaac Kaliati kaamba komwetsa zigoli zisanu ndi zitatu mu ligiyi.

Wanderers ndi yachiwiri pa ndandanda wa matimu mu ligiyi ndi ma point 34 pamasewero 18 pomwe Silver ikutsogola ndi ma point 40 pamasewero 16.

Wolemba Peter Fote

Team manager wa Wanderers Steve Madeira kusangalala ndi Kaliati.

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Please disable your adblocker or whitelist this site!