Mtsogoleri wa timu ya Mighty Mukuru Wanderers a Thom Mpinganjira wati ndi wokondwa ndi m’mene timuyi ikuchitira pa masewero ake a mu ligi ya TNM.
A Mpinganjira ati apempha osewera a timuyi kuti adzipereke kwatunthu pa masewero omwe atsala nawo kuti apitilire kupereka mpikisano wa ukulu ku timu ya Silver Strikers yomwe ikutsogola pakadali pano.
Iwo ayamikiranso osewera wa pakati wa timuyi Isaac Kaliati kaamba komwetsa zigoli zisanu ndi zitatu mu ligiyi.
Wanderers ndi yachiwiri pa ndandanda wa matimu mu ligiyi ndi ma point 34 pamasewero 18 pomwe Silver ikutsogola ndi ma point 40 pamasewero 16.
Wolemba Peter Fote
Team manager wa Wanderers Steve Madeira kusangalala ndi Kaliati.
MALAWI
FREEDOM
NETWORK
United for Freedom, Justice and a Better Malawi
Airtel Money
0994095804
Mpamba
0881428759
FDH Bank
Acc No:
1400000670385NBS Bank
Acc No:
10118988Thank you for your support!