Masewero alero atulutsa zigoli khumi ndi ziwiri

Zigoli khumi ndi ziwiri ndizomwe zagoletsedwa masewero omwe analipo lachitatu pa 25 September 2024 mu TNM Super league.

FCB Nyasa Big Bullets yagonjetsa Creck Sporting Club 3-2 pamasewero omwe anachitikira pa bwalo la Kamuzu mu nzinda wa Blantyre.

Maxwell Gasten Phodo, Babatunde Adepoju komanso Ernest Petro anagolestera mapale, pamene Muhammad Sulumba anagoletsa zigoli ziwiri yekha kuti masewero athere 3-2.

Masewero ena omwe analipo pa bwalo la Balaka, Kondwani Chilembwe, Richard Lapson komanso Clever Chikwata anagoletsera Bangwe All Stars kuti igonjetse igonjetse Baka City 3-0.

Peter Katsonga anali katswiri ofunikira pamene anagoletsa zigoli ziwiri yekha kuti timu yake ya Mafco FC igonjetse Mighty Tigers 2 kwachilowere pamasewero omwe anachitikira pa bwalo la Chitowe m’boma la Nkhotakota.

Ndipo pa bwalo la Civo, Christopher Mtambo komanso Gregory Nachipo anagoletsera Kamuzu Barracks kuti igonjetse Premier Bet Dedza Dynamos.

Silver Strikers ndiyomwe ikutsogola pa m’ndandanda wa ma timu ochita bwino mu TNM Super league ndi mapointi 48 pamasewero 20 omwe asewera, pomwe Mighty Mukuru Wanderers ili panambala yachiwiri ndi mapointi 41.

  • Related Posts

    Is the Vice President of Malawi Supposed to Use Public Resources for Private Life Affairs? A Litmus Test for “Return to Proven Leadership”

    Opinion By Donald Malanga In the shadows of our nation’s hospitals, where medicine cabinets stand empty, and in markets where food prices soar beyond reach, a question of moral leadership…

    Investigative Report: The Lobin Lowe “Butchery” Fertilizer Scandal and Its Legal Aftermath

    By Investigative Desk 1. Summary of the Scandal In 2022, Malawi’s Affordable Inputs Programme (AIP) was rocked by a procurement scandal in which the Ministry of Agriculture paid approximately K750…

    Leave a Reply

    Your email address will not be published. Required fields are marked *

    //otieu.com/4/9370459