Zipani zina zotsutsa boma m’dziko muno zati palibe cholepheretsa ziwonetsero zomwe akonza kuti zichitike tsiku la lero.

Izi zikudza ngakhale apolisi adati lero ali ndi ntchito zina zoti agwire kotero sapezekako ku ziwonetserozi.

Zokambirana pakati pa mbali ziwirizi zalephera kubwera ndi mfundo imodzi ndipo agwirizana kusagwirizana.

Zipanizi zomwe n’kuphatikizapo UDF, UTM, AFORD, DPP komanso EFP zati sizokhutira ndi kagwiritsidwe ntchito ka bungwe la MEC komanso NRB.

Kotero akuyembekezeka kuchititsa ziwonetsero ku Lilongwe zomwe akufuna kuti adindo ena ku MEC atule pansi maundindo awo komanso kusintha momwe ndondomeko ya kalembera wa zisankho ikuyendera.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *