By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Is it possible for Kabambe to win 2025 presidential elections without forming electoral alliances?
- Kabambe’s economic legacy remembered by UTM’s Felix Njawala at Masintha Rally
- Chilima Had No Confidence in MCP Alliance, Says Njawala
- MCP Aspiring MP Chisale Launches Free Mobile Clinic in Kasungu Central to Ease Healthcare Access
- Kunkuyu Urges Media to Uphold Professionalism Ahead of 2025 Elections
- Safe homes crucial in children rehabilitation -Irish Rule of Law
- The Great Lie: NEEF and the Myth of Economic Empowerment under the MCP Government
- MACRA Urges Broadcasters to Promote Peaceful Messaging Ahead of Elections
- Chakwera Calls for Unity, Condemns Tribal Politics and Violence in Malawi
- Kalindo congratulates Police Commissioner Noel Kayira
- 127 days to the ballot: MEC highlights key electoral conduct rule ahead of 2025 Malawi General Elections
- Vitumbiko Mumba Takes MCP to Court Over Mzimba Central Primary Elections Dispute
- Mangochi Businessman Wins K8.755 Million in Azam TV Grand Raffle Draw
- Grill Like a Pro with Ekhaya Meats’ Grill-Ready Patties!
- Counsel Sylvester James Ayuba Writes to President Chakwera: “Please, Your Excellency, Come to Work ”
- Pope Leo XIV Pays Homage to Mary and Late Pope Francis in Spiritual Pilgrimage to St. Mary Major
- The unlikely rise of Pope Leo: A humble shepherd called to the world stage
- The unlikely rise of Pope Leo: A humble shepherd called to the world stage