By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Retired Judge Mwaungulu Demands Criminal Prosecution Over Chilima Plane Crash
- A New Dawn at Mpira Village: Yvon Avry Steps In to Redefine Malawi’s Football Future
- DPP to hold Mtandire–Mtsiliza appreciation rally after securing community support
- Kalindo calls government to revisit councilors salaries
- Comrade Ntanyiwa vows to expose corrupt ministers in the DPP
- Vice President Jane Ansah Vows Swift Action to Protect Vulnerable Families During Northern Region Lean Season
- Gazette Media donates K0.5 million to Football Journalists
- NBM plc donates 84 desks to Namitambo Primary School
- Why Peter Mukhito’s Record Offers Malawi Renewed Confidence in National Security
- The great escape: Former MCP ministers flee Malawi amidst corruption probe
- Korea Pledges Stronger Partnership With Malawi in Agriculture, Health, Digital Skills, and Renewable Energy
- Mwaungulu pledges to work with all to develop Katoto-Chibavi Ward
- From suppression to empowerment: Dr. Florida Banda’s triumphant return to leadership
- Game On, Malawi! Malawi’s’S First Ever Cyberexpox On The Horizon
- Bakili Muluzi TV Issues Warning Over Fake MCP-Linked Pages and WhatsApp Groups
- Gertrude Mutharika Shares Warm Morning Message with Followers
- Inua Advocacy says it is aware of alleged spies from Rwanda
- Malawi, India Reaffirm Strong Bilateral Ties During Courtesy Call

















