By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Mai Halima Girls Records 100% Pass Rate in 2025 MSCE Exams
- DPP Deputy Leader Joseph Mwanamveka Urges Chiradzulu Residents to Vote Peter Mutharika to Restore Wealth
- Peter Mutharika Claims He is Malawi’s Only Leader Who Can Cure the Nation’s ‘Cancer’
- Aford’s Enock Chihana Promises K5 Billion Development Boost Per Constituency if Mutharika Wins
- Angela Muluzi Launches Whistle-Stop Rallies in Blantyre to Boost Atupele Muluzi’s Campaign
- Reflects on Current Opinion Polls as Just Propaganda, Ill-Timed and a Recipe for Post-Election Violence
- Navigating the 2025 Malawi Presidential Election: A Crucial Choice Between Proven Leadership and Uncertain Continuity
- Chakwera’s calculated sabotage: How Malawi’s president is engineering electoral chaos and igniting the flames of conflict
- Valuation tribunal now operational, promises fair property assessments
- Toyota Fortuner 2025 Rolls Out Globally with Premium SUV Styling, Updated Interior Features and Futuristic Engine Options
- Lilongwe City Nankhaka constituency PwDs to vote for Grace Chupa
- Bwalo la Chewa Foundation mourns Reverend Flywell Somanje
- Kamphangala advises Chimwendo to stop commenting on surveys
- MBC DG describes Usi as a confused man
- Concerned Citizens Give President Chakwera Two Days to Approve DPP Commissioner at MEC
- SULOM Cracks Down on Unregistered Players Ahead of Malawi Super League Matches
- Angela Muluzi Backs Atupele Muluzi’s Vision for a Corruption-Free Malawi
- Chakwera’s waning popularity signals a nation in search of fulfilled promises