By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Former Mzuzu City MP Mwamlima congratulates Kaweche, pledges support
- Kalindo advises politicians not to take citizens for granted
- Jane Ansah as Vice President: Balancing Competence, Credibility, and Public Expectations
- Imran Jumbe Congratulates Alfred Gangata on Appointment as Minister of State
- Questions Over Wealth and Power’: Allegations Swirl Around Former SPC Colleen Zamba’s Tenure
- BMTV thanks Malawians for working together to oust MCP
- Kalua condemns MCP for turning Kamuzu Palace into shame
- TFM Centre of Excellence Donates K10 Million to IPMM for 2025 Annual Lakeshore Conference
- Bridging the Divide: Enoch Chihana’s Strategic Role in Malawi’s Executive
- A Test of Vision and Accountability: Decoding President Peter Mutharika’s New Cabinet
- Alfred Gangata: A Fresh Face in the State Ministry Amid Public Anticipation
- Pastor Moses Shumba says Malawi is now free under Mutharika
- Limpopo FM urges Malawians to build the country
- Fresh and Healthy: Enjoy Our New Lettuce & Cucumber Salad Today!
- Joseph Mwanamvekha: Steering Malawi’s Financial Ship Amid High Expectations
- President Mutharika’s Cabinet Shake-Up: Balancing Politics, Experience, and the Promise of Renewal
- Government Shuts Down Salima Sugar Company Over Financial and Management Concerns
- Mutharika Praised for Promoting Regional Balance in Security Appointments