By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Ben Longwe urges Malawians say “NO” to endorsing Chakwera
- Malawi politicians prioritizes winning elections over truth
- Mutharika showers Blantyre Synod pastors with cash and promises
- MEC clarifies voter transfer process
- NICE urges journalists to exercise professionalism
- Chihana Sparks Controversy with “Minister of Pit Latrines” Remark
- Chakwera panics, invites Blantyre Synod pastors to luncheon
- Kampanikiza Wins MCP Primary Election for Dedza Boma Constituency
- Civil Society Groups Defends President Chakwera’s State of the Nation Address
- Boycott September Elections for Transitional government if Demands of The People On MEC Falls in Deaf Ears
- Ali Blessings Eid Agawa Ufa Ku Mabanja Omwe Akuvutika Ndi Njala
- President Chakwera engages Malawian Youth in Digital Town Hall Forum
- Former President Mutharika engages with clergy as he prepares for a political comeback
- Malawi hit by cyclone Chakwera: MP’s scathing remark sparks frenzy in Parliament
- Jumah says Malawians are to blame for the country’s mess
- Improved implementation expected for the Last Mile Infrastructure Project
- Malawi at a crossroads: A call for new leadership
- Minister of health officially opens state-of-the-art Mwangala health centre in Dowa district