By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Mwanamvekha Secures $51 Million in Single Foreign Trip as Malawians Praise Results-Oriented Leadership
- Next Generation: Harnessing Innovation, Education, and Leadership to Shape Malawi’s Future
- Kelly Kay, Eli Njuchi, others to spice NBM plc family day gig in LL
- Hon. Suleman Emerges as Front-runner for Malawi Parliament Speaker Post
- 300 Fuel Tankers Bound for Malawi to Ease Persistent Shortages
- Brigadier Charles Kalumo Stripped of Three Government Vehicles Gifted by Former President Lazarus Chakwera
- Namalomba claims Malawi’s economy is a maize economy
- Jumbe says political agreements are not mere signatures on paper
- Mulli Engages Aliko Dangote for Fertilizer and Fuel Deals to Boost Malawi Economy
- Malawi Secures Major International Support to Boost Economic Stability
- Mwanamvekha Vows Crackdown on Black-Market Forex and Fiscal Waste to Restore Malawi’s Economy
- Allan Ngumuya: Four Decades of Gospel, Faith, and Musical Evolution
- Africa Hosts Nearly Half of the World’s Armed Conflicts, Says ICRC
- K500 Million Vanishes in Mzuzu Airport Renovation Scandal — Malawians Demand Answers
- Concerned citizen claims MCP has learnt many lessons from 2025 politics
- Former Chakwera Regime and Malawi Congress Party Linked to Maheu Procurement Scandal
- FAM president motivates the Scorshers
- President Mutharika Urged to Revoke Nir Ges’ Diplomatic Passport Amid Outgoing MCP Scandal

















