By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Mayamiko Nkoloma Embraces MEC Appointment with Sense of National Duty
- Chakwera Recalls Parliament to Tackle Electoral Law Gaps
- Rastafarians Call for Peace and Unity Ahead of Malawi Elections
- Atupele Muluzi – A legacy refined, a vision reimagined for Malawi’s future
- DPP and AFORD Sign Political Alliance Ahead of September Elections
- TNM Launches 5G Network in Lilongwe: Ushering Malawi into a New Era of Connectivity
- A vision for the future: What Malawi stands to gain under President Atupele Muluzi
- Lilongwe Turns Yellow as Atupele Muluzi Submits Nomination Papers at BICC
- Atupele Muluzi Rallies Youth Leadership as He Submits Presidential Nomination
- MCP Set to Launch Manifesto in Mangochi as 2025 Elections Approach
- Atupele Muluzi submits nomination papers to MEC, cementing UDF’s 2025 Presidential Bid
- Kamphangala describes the dissolved 2019-2025 Parliament, the worst
- Chimbanga writes food for thought on DPP running mate
- Bakili Muluzi TV vows to expose all running mates—Jane Ansah in the spotlight
- “History Is the Best Teacher”: Bakili Muluzi TV mocks UTM and MCP supporters over Jane Ansah’s nomination
- Bakili Muluzi TV hails DPP’s Running Mate pick as more educated than MCP and UTM leaders
- Professor Mutharika hails Jane Ansah as a woman of integrity and key partner in nation rebuilding
- DPP, AFORD, and NDP seal historic electoral alliance ahead of 2025 Polls