By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Japan Poised to Power Malawi’s Infrastructure Boom
- Concerned citizen says only the law will arrest Chakwera
- African Journalists Urged to Promote Gender in Climate Change Reporting
- Purezidenti Mutharika Adzatsegula Malangizo a Dziko mu State of the Nation Address
- President Mutharika to Outline Vision for Malawi in State of the Nation Address
- CDEDI Yachenjeza: Chigamulo cha Supreme Court pa Finance Bank Chitha Kuipitsa Chuma cha Malawi
- CDEDI Warns Supreme Court Ruling on Finance Bank Could Wreck Malawi’s Economy
- Suleman Chitera Applauds President Mutharika’s Bold Move to Cut Ministerial Travel
- Zimbabwe Moves to Redraw Presidential Rules, Raising Fears of Power Extension to 2030
- Bungwe la Makanjira Development Foundation Lafuna Kufotokozedwa Momveka Bwino pa Ntchito ya Mseu wa Makanjira
- Makanjira Development Foundation Demands Clarity on Long-Delayed Makanjira Road Project
- Mutharika akhomera nduna pa ulendo wa M’dziko pamene Boma likutaya ndalama zambiri
- Mutharika cracks the whip on ministers’ travel as government bleeds cash
- BMTV claims adjournment is used by judges to be rich
- 20 Years of Justice Delayed: Who Benefited from the Finance Bank Case Dragging On?
- A National Appeal for Fair Government Purchase of Maize from Local Farmers- Jumbe
- Public Appointments Committee Approves George Partridge as Reserve Bank Governor
- Malawi Hails Japan Support as Lilongwe, Tokyo Deepen Bilateral Ties













