By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- ACB Cracks Down on Passport Corruption as 21 Immigration Complaints Trigger Probe
- Trade Minister hails MAGLA on responsible gambling initiatives
- JB Calls on President Mutharika for U.S. Embassy Appointment
- No more transfers, only firings: Phiri issues stark ultimatum to Zomba City council staff
- Government Rallies New Roads Authority Board to Drive Accountability, Quality and Faster Infrastructure Renewal
- Education for Generations: Lindian Resources Steps Up as Government Expands Free Schooling
- Salima Sugar Accused of Choking Farmers as K1.8 Billion Debt Sparks Protest in Lilongwe
- Government Reaffirms Commitment to Quality Urban Infrastructure
- Why Strategy Without Communication Is Silent Failure
- Homeland Security to Address Media on Recent Interventions
- State moves to overturn High Court orders in Chimwendo Banda case, Alleges abuse of Judicial process
- Minister Puts Airtel Malawi on Notice Over Persistent Service Failures
- Kalindo calls government to cushion Malawians amid fuel price increases
- AG to challenge Chimwendo Banda’s judicial review case
- US Proceeds With WHO Exit, Triggering Global Health Concerns
- China Strikes Without a Shot: The Economic Blowback that Has the United States Reeling
- PCL, Press Trust donates K142 million relief items to Dwangwa flood victims
- Justice for Sale? Malawi First Takes Aim at the Courts Over Chimwendo Banda Ruling

















