By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Malawi Triathlon Tournament Boosts Sports Development in Nkhatabay
- Young Builders Challenge to Reward Top Entrepreneurs in Lilongwe
- Nankhumwa demands respect for Professor Arthur Peter Mutharika, Getrude Mutharika
- Chakwera’s silence abroad as his inner circle faces the cells
- BMTV says Mumba, Chimwendo Banda deserve to be arrested
- Malawi Secures Major $15 Million Kuwait Grant to Boost Infrastructure and Economic Recovery
- Nyamilandu Pledges Ambulance to Improve Emergency Health Care in Chididi
- Major Review Finds Limited Evidence Supporting Medical Cannabis for Common Conditions
- No retreat, no surrender: the wheel has turned
- MCP Spokesperson Jessie Kabwila Arrested as Political Tensions Escalate
- Loyalty: the currency that sustains real political power
- When the State House Became a Vestry: How Diplomatic Missions Were Turned into Feeding Troughs
- MCP comeback appears increasingly unlikely
- BMTV tells Mhango one reason – fresh inquiry
- Kamphangala thanks MCP youth for shunning demos meeting
- Malawians Demand Transparency as Tollgate Revenues Rise but M1 Road Deteriorates
- MAM Blasts MCP Government for Snubbing Eidul Adhuha
- Police to Unmask Charges Against Mumba, Chimwendo Banda After Night in Custody

















