By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Chipani cha Malawi Congress Party chatilephera ndipo chinabwera kuzangoononga chuma cha dziko
- Fake news alert: MEC refutes false claims about Chairperson Mtalimanja’s resignation
- Presidential Candidates to Face Youth in National Debate Ahead of 2025 Polls
- Rushing into the unknown: Why Malawi must rethink Smartmatic and the 2025 electronic voting gamble
- Desperation on the Highway: Women Collect Maize Spilled from Moving Truck as Hunger Bites Malawi
- Rev. Kawalala Urges Unity and Vision Ahead of DLGF Conference on Revitalising Malawi’s Economy
- FDH Bank Attributes K74 Billion Profit to Staff Dedication Amid Economic Challenges
- Venezuela vote: Turnout figure ‘tampered with’
- Odya Zake Alibe Mlandu Now Fully Registered, Says Secretary Kondowe
- OXFAM to Implement Improving Communities’ Livelihoods Resilience for Healthy Lives in Dowa
- Chipani cha Odyazake Aibe Mulandu, chavomerezedwa mwalamulo — A Happy Kondowe atsimikiza
- Mtalimanja will declare you winner through Smartmatic rigging not votes- Kalua tells Chakwera
- Kamlepo Kalua joins Chakwera that he has won the elections
- Kalindo says “Walk-in interviews” exposes leadership failure
- Tata Sumo 2025 Model 7-Seater Car Launched at the Price of a Pulsar Bike – Comes with 2956cc Engine and Great Mileage
- Kenyan president apologies to Tanzania over deportation row
- When presidents say “I’m Sorry”: A lesson in leadership and humility
- Malawian youth, wake up – it’s time to reclaim your future!