By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Chakwera Urges Malawians to Endure as K62 Billion Spent at State House
- Newton David Kambala: The Trusted Advisor Behind UTM’s Political Strategy
- Malawians Will Vote for Arthur Peter Mutharika Even If He Campaigns on a Wheelchair
- Healthcare in crisis: MCP’s drug shortages leave Malawians suffering
- FDH Premier Netball League set to launch in Blantyre, ushering in a new era for Malawian Netball
- Nation newspaper reports K17 trillion stolen, a worrisome news
- DPP Governor claims Chakwera already campaigned for Mutharika
- Malawi Politics: Friends of Atupele Muluzi Demand Apology from DPP’s Sameer Sulemani Over Leader Attacks
- Epay Revolutionizes Digital Payments in Malawi
- UTM forms alliance with PPM in strategic political move
- Sameer Suleman criticizes Chakwera over treatment of the Late Sidik Mia
- UTM and DPP Join Forces to Safeguard Electoral Integrity in Malawi
- FDH Bank Donates K10 Million to Support Malawi Engineering Institute Conference in Salima
- Local Government Elections in Msitu Ward suspended following candidate’s death
- MEC releases official list of approved parliamentary candidates for 16 September Elections
- APTL Global Limited Hosts Comprehensive IFRS Masterclass Workshop to Elevate Financial Reporting Standards
- Lilongwe, it’s give away time
- Dr Jane Ansah Leads DPP Campaign in Nchalo