By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Vice President Ansah, Norwegian envoy chart new path for stronger bilateral cooperation
- HRDC Accused of Hypocrisy Over Recent Statement on National Service Challenges
- Netizens Raise Concern Over Zambian Music Industry’s Silence as General Kanene Laid His Daughter to Rest
- Kalindo advises Vice President to check ghost workers
- South Africa Deports 490 Malawians for Immigration Violations
- Chihana Calls for Presidential Intervention in Kasasile Land Dispute with MDF
- High Court Orders MEC to Release Lilongwe Mtandire–Ntsiriza Election Results
- FCB plc gives K210 million for food relief
- Silver Strikers Pocket K45 Million as 2025 FDH Bank Cup Final Rakes in K112 Million
- Mo626 Varsity Games targets unearthing university talent
- World Bank Reaffirms Support to Malawi Amid Economic Challenges
- MCP past history a contributing factor to losing elections
- Norman Chisale Donates Motorcycles and Maize Flour to Communities in Ntcheu
- Vice President Enoch Chihana Leads Remembrance Day Ceremony in Mzuzu
- Malawi Commemorates Poppy Day in Zomba with Wreath-Laying Ceremony
- Malawi’s Governance Under Pressure: Fiscal Cuts, Legal Disputes, and Security Partisanship Challenge State Institutions
- Riot and Arson in Chingola as Presidential Visit Turns Violent
- Concerned citizen dismisses politics arresting, re arresting MCP thugs

















