By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Kaweche Pledges Sustainable Development for Mzuzu City South East Constituency
- The right attitude towards truth and accountability
- NRFA Elections Voting Suspended Amid Chaos
- Chavura re-elected National Youth Football Association chairKONDWANI KANDIADO
- Jumah joins Chakwera to remove failed Ministers
- Ben Longwe claims no truth about Chikangawa inquiries
- NRFA Elections Voting Suspended Amid Chaos
- Chakwera’s web of lies: How the President’s SONA betrayed public trust
- President Chakwera caught with his lies in the 2025 state of nation address
- Chakwera’s SONA: A masterclass in blatant lies and deception
- PDP President Kondwani Engages Grassroots Leaders in Lilongwe
- A nation betrayed
- Cooking oil prices skyrocket to MWK 195,000, sparking calls for leadership resignation
- President’s misattribution sparks outrage: COFO demands recognition for clinic construction
- SONA full of lies: Chakwera’s embarrassing week
- Two die in separate road accidents in Mangochi
- President Chakwera highlights progress in Nsanje during state of the nation address
- President Chakwera’s vision for Chitipa: A future trade corridor and major city