By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Malawi’s 2025 Presidential showdown: Is Chakwera still the answer or is it time for Mutharika’s return?
- Mukhito pledges transformation for Lilongwe City Centre if DPP returns to power
- Kalindo says Malawi is a country of shame
- Kamlepo Kalua claims Malawians are not against Chakwera
- Chimwemwe Idana Bids Farewell to Silver Strikers, Set for Zanaco FC Move
- Mapingo CDSS Students Protest K12,000 Exam Fees
- Malawi Government and Huawei Begin Smart Village Construction in Lilongwe
- Dr. Dalitso Kabambe Pledges Economic Revival on Whistle Stop Tour in Machinga
- Paul Aaron Gadama slams Chakwera’s forex mismanagement, urges Malawians to rally behind DPP
- YAS challenges Chakwera to publicly guarantee safety of protesters and opposition figures
- Opinion, The unfinished business of street vending in Lilongwe: Seeking lasting solutions to a growing urban crisis
- DPP’s Alfred Gangata declares ‘Holy Smoke’ with incoming Gen-Z Demos in Lilongwe
- Confusion over parking spaces in Lilongwe raises public concern
- Malawians are to blame for their poor choices: A case of Chakwera’s poor leadership
- Chakwera condemns the violence from demos in Lilongwe
- PIH to implement Health Systems Strengthening for NCD diseases
- EAM demands joint security inquiry into Lilongwe attacks, urges political responsibility
- Peter Mukhito Ayambitsa Kampeni ku Kauma Pomwe DPP Ikachita Msonkhano wa Ndale