
Tikalembetse A Malawi Mkaundula wa Zisankho mphamvu ya kusintha dziko LINO ili mmanja mwathu
By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Mwanamvekha Holds Key IMF Talks in Gambia
- FCB Says Swipe and Dash Promotion Boosted Digital Banking Uptake
- Maranatha International to Open Hospitals Across Malawi
- Bobe’s murder case commences with two witnesses testifying
- Kamphangala says happy with foot soldiers concerns reaching Mutharika
- UK-Malawi Business Roundtable Boosts Hopes for Increased Trade and Investment
- Chithyola Banda Calls for Protection, Compensation for Malawians Affected by South Africa Attacks
- Mwawi Kumwenda to Join Malawi Queens Ahead of 2026 Commonwealth Games
- NBM plc concludes ‘Guess the Jersey’ challenge with 20 more winners
- Power Crisis in Malawi: Businesses Lose Millions as Electricity Shortages Disrupt Operations
- After South Africa Attacks: How Repatriated Malawians Are Rebuilding Their Lives
- 2030 Malawi Elections: Political Parties Begin Early Strategies as Political Battle Lines Emerge
- NFCAM Welcomes Wedson Nyirenda
- ERFA and SRFA Endorse FAM President Fleetwood Haiya Ahead of 2027 Elections
- Senior Chief Mposa Demands Answers Over Missing K100 Million Hunger Relief Funds in Machinga
- Parliament Urged to Tackle University Fees, Data Costs and Xenophobic Attacks
- Malawi at 62: Comrade Imran Jumbe Questions Independence Celebrations
- Malawi at 62: UDF President Atupele Muluzi Calls for ‘Third Liberation






























