By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Bangladesh Government Saves ‘Donald Trump’ Cow from Eid Slaughter After Viral Fame
- Malawi Seeks Increased AfDB Support as Mwanamvekha Holds High-Level Talks with Bank President in Congo
- Mo626 Intercollege Social Weekend shakes Mzuni
- NBM plc celebrates Africa Day in style
- President Peter Mutharika Calls for Unity and Peace as Muslims Celebrate Eid al-Adha in Malawi
- US Launches Fresh Strikes on Iran as Strait of Hormuz Crisis Deepens
- Iran war live: US strikes Iranian site; Kuwait targeted by missiles, drones
- Malawi, IMF to Begin Extended Credit Facility Talks in June
- IMF Talks Return as Malawi Battles Economic Turbulence, Mwanamvekha Rules Out Devaluation Agenda
- Napoleon Dzombe Nears Completion of Fertilizer Factory in Dowa as Malawi Eyes Local Production Boost
- Eid Al-Adha Marked by 30-Cattle Donation from Dr Jane Ansah Foundation to Malawi’s Muslim Communities
- Malawi, IMF Set for Crucial June Talks on New Economic Reform Programme
- Corruption in Malawi’s Public Hospitals Undermining Health System, Journalists tell Parliament
- Will ADMARC Be Called The Granary For Farmers Again?
- Muslims in Malawi to Observe Eid Al-Adha Tomorrow as MAM Calls for Support Amid Cattle Movement Restrictions
- Biography of Aaron Gadama
- MCP–UTM Memorial Row Over Saulos Chilima Sparks Political Backlash as Analyst Warns of Ill-Timed Dispute
- Ekhaya Farm Foods Fresh Oranges Deliver the Perfect Vitamin C Boost
MALAWI
FREEDOM
NETWORK
United for Freedom, Justice and a Better Malawi
Airtel Money
0994095804
Mpamba
0881428759
FDH Bank
Acc No:
1400000670385NBS Bank
Acc No:
10118988Thank you for your support!

















