Khansara wa MCP a Gabriel Mwaungulu atula pansi udindo wawo

IMG 20230612 WA0004

Khansala wa chipani cha Malawi Congress Party (MCP) wa Ward ya Chibavi East a Gabriel Mwaungulu atula pansi udindo wawo ndipo walowa chipani cha Alliance for Democracy (AFORD).

Mwaungulu adalengeza kusiya ntchito yake Lamulungu pa msonkhano wokumbukira zaka 30 womwe a Enoch Chihana adakonza pa Chibavi Ground mumzinda wa Mzuzu.

Khansala walonjeza kuti agwira ntchito molimbika pokopa anthu kuti avotere Chihana ndi AFORD pa chisankho chomwe chikubwera cha 2025.

Panopa bungwe la AFORD likuchita misonkhano m’dziko muno zisankho zisanachitike.

Chipanichi chikuyembekezeka kuchita msonkhano wawo wachisankho mu Seputembala

0 0 votes
Article Rating
Subscribe
Notify of
guest
0 Comments
Oldest
Newest Most Voted
Inline Feedbacks
View all comments
//otieu.com/4/9370459
0
Would love your thoughts, please comment.x
()
x