By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Mutharika Assures IMF of Swift Action to Resolve Malawi’s Economic Crisis
- Calls Mount for Full Audit as Critics Accuse Former President Chakwera of Mismanaging Billions”
- CDEDI Demands Accountability from Former President Chakwera Over K67 Billion Expenditure
- CDEDI Says Former President Chakwera Does Not Deserve Retirement Benefits
- Minister Navicha Warns That Digital Technology Is Intensifying Gender-Based Violence in Malawi
- Norman Chisale Reflects on a Defining Moment Before Malawi’s Election Outcome
- Press Corporation Donates K300 Million as Govt Moves to Tackle Root Causes of Food Insecurity
- Sharriff, Chinkhandwe shine at NBM plc Seniors Golf Tourney
- The Walkers in QECH Children’s Cancer fundraising walk Dec 6
- MCP takes up national budget resources for personal gains
- K67 Billion Gone: Investigating the Rapid Depletion of State House Funds
- Calls Grow for Cost-Cutting Measures in Presidential Travel and Allowances
- Chihana Reaffirms Government’s Commitment to Food, Fuel, Forex & Fertiliser Stability at Chikwawa Rally
- DPP Welcomes Two Aspiring Candidates for Rumphi Central By-Election
- G20 Leaders Back Fairer Global Economy as Italy Commits to 50% Debt Relief for Africa
- Vice President Jane Ansah Begins High-Level Diplomatic Mission in Angola
- BMTV claims State House spent K115 billion for Chakwera
- Comrades Ntanyiwa, Mangochi praises Mathanga for fuel supply
















