By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Chithyola Banda: Between Allegations and Political Undercurrents
- Kalindo thanks Mutharika for Chilima’s death fresh inquiry
- CDEDI Blasts Chakwera Era as “Malawi’s Worst Mistake,” Says Mutharika Comparison an “Insult”
- CCYCDO Strengthens Community Ties Through Visit to Disabled Individuals in Chiradzulu
- Gulf in Flames: Iran’s Retaliatory Blitz Shakes U.S.–Israel Alliance and Redraws the Balance of Power
- Msonda claims corruption cannot happen in government without him being aware
- Kamphangala plead with Kenyatta to revoke panga wielding thugs bail
- NBM plc unveils Mo Excellence programme for tertiary students
- MAM distributes food to Muslims in Nkhotakota
- Global War Shock: South Africa Hikes Fuel Prices as US–Israel–Iran Conflict Drives Up Costs
- PressCane donates K50 million in food relief to flood victims in Chikwawa
- Business columnist says Mwanamvekha facing difficult task of restoring economy
- NBM Platinum Employee Award winners return home safely after regional unrest
- Starmer Warns of Escalation as Iran Intensifies ‘Reckless’ Strikes After Khamenei Killing
- BREAKING: Israeli PM, Benjamin Netanyahu’s Office Reportedly Attacked In Surprise Missile Attacks
- Makanjira Foundation Demands Action as Government Allocates K664 Billion for Road Projects
- ERFA Hails First-Year Gains, Doubles Team Subventions Amid Refereeing Concerns
- MCP member urges government to speed up Chilima’s death investigations





















