By Comrade jumbe
Pa chichewa pali mawu amatero kuti tsogolo ndi la iwo amene akukonzekera lero ,
Abale ndi alongo lero ndi mwayi wina wofunikira kwambiri kwa nzika iliyonse yomwe ikufunira zanwino dziko lino .
Mmene kalembera wa zisankho afika ku mapeto uwu ndi mwayi wathu womaliza wokonzekera kusintha komwe tonse amalawi takhala tikuyembekezera.
Chisankho chomwe chikubwerachi sichinthu chongochitika mwachizoloŵezi monga mwa nthawi zonse koma ndi nthawi yofunika kwambiri m’mbiri ya dziko lathu.
Kukhala chete osatenga nawo gawo liri lonse pa chisanko pamene ena akusankha tsogolo lathu ndi kuzimpwanyila tokha ufulu okonza tsogolo la dziko lathu chifukwa mphamvu zobweretsa kusintha zili mu voti yathu ndipo uwu ndi mwayi wotsiriza popeza kulembetsa kwa mec kwafika kumalecheleche.
Tiyenela kukumbukira kuti mtsinje umadzadza ndi dontho limozi limozi kulembetsa kwanu kungawoneke ngati kochepa koma kukalumikizana ndi mamiliyoni ena kumakhala mphamvu yomwe palibe munthu olo boma linganyalanyaze.
Ndikumema inu nonse amalawi kuti pitani mukalembetse mukawundula wazisankho auzeni anzanu akubanja lanu ndi aneba kuti achitenso chimodzimodzi.uwu ndi mwayi wathu kuti tichotse omwe alephera ndikusankha atsogoleri omwe adzayike miyoyo ya anthu patsogolo.
Chisankho cha mu September sichisankho chabe chifukwa amalawi talira kokwana ndipo tikulira kotero ndi nthawi yathu yobweretsa kusintha komwe takhala tikudikirira.
Kalembetseni lero ndikuteteza liwu lanu pokonza tsogolo la dziko lathu. mphamvu ili m’manja mwathu tiyeni tigwiritseni ntchito mwanzeru .
pamodzi tingathe
- Timeline Questions Emerge in Malawi’s Chikangawa Plane Crash Inquiry
- Catechist Urges Christians in Nathenje to Prioritize Prayer and Thanksgiving
- Mthunzi Trust inspires Maya PVT Secondary School students through career and entrepreneurship talk
- Malawi Waits for Chakwera’s Testimony as Chilima Death Inquiry Enters Critical Stage
- Chikangawa Plane Crash Inquiry Uncovers New Leads as Parliamentary Committee Deepens Investigation
- Equatorial Guinea Government Resigns After Failing Development Targets
- NBM plc launches BankNet360 to enhance digital banking experience
- National Bank of Malawi Launches BankNet 360 to Revolutionize Digital Banking Services
- Chilima air crash: unanswered questions continue to haunt Malawians
- SHOCKING COMPARISON: What MK100,000 Can Buy in Malawi Today Compared to Just Two Years Ago
- Who Would Malawians Vote For If Elections Were Held Today? Looking Ahead to the 2030 Elections
- Malawi Tobacco Rejection Rate Remains High at 64% as Sales Drop
- Mangochi Girl Duwama Muhammad Wins Full Scholarship to Study at Sharda University in India
- Support Malawi Freedom Network: help us keep the voice of the people alive
- Dutch National Wim Akster Claims Malawi Police Forced False Confession in Sexual Abuse Trial
- Experts Warn Against Hasty Malawi Kwacha Devaluation Amid Exchange Rate Unification Calls
- Lionel Messi Makes History with First World Cup Hat-Trick as Argentina Defeat Algeria 3-0
- Monkey Bay Set to Become Malawi’s New Secondary City as 10-Year Development Project Begins




























Leave a Reply