Sat. Apr 27th, 2024

Abida Mia acheza ndi anakubala pa chipatala cha Ngabu

By Suleman Chitera Oct15,2022

Wolemba: Leo Mkhuwala

Phungu woimila dela la Chikwawa Nkombedzi ku nyumba ya malamulo, Mayi Abida Mia watsindika kufunika kwa anakubala pamene anakayendera amayi omwe abereka kumene komanso ena omwe akudikilira kubereka pa chipatala cha Ngabu m’boma la Chikwawa chomwe chiri m’dela lake.

Mia yemwenso ndi nduna yowona za madzi ndi ukhondo, anafika pa chipatalacho ndi mphatso zosiyanasiyana monga zitenje, shuga ndi zakumwa zomwe adapereka kwa amayi osachepera makumi awiri, anati kwa mwana aliyense, nakubala ndi wofunika kwambiri chifukwa chobereka mwana ndi kumulera, popilira zowawa zambiri kufikira atakula.

“Palibe mphatso ina ya mtengo wapatali kuposa mphatso ya moyo yomwe nakubala amaipereka kwa mwana wake,” anatero Mayi Mia ndi kupitilira: “N’chifukwa chake mwana aliyense pa tsiku la anakubala akuyenera kukumbukira mayi wake chifukwa cha mphatso ya moyo komanso ntchito yaikulu yolera mwana yomwe mayi amagwira.”

M’chipinda cha matenite pa chipatala cha Ngabu, nkhope za amayi zinali zowala ndi chimwemwe pamene phungu wawo anafikira mayi aliyense mwapadera ndi kucheza naye komanso kunyamula khanda m’manja mwake ngati njira imodzi yogawana nawo chimwemwe pa tsiku la anakubala.

Pa 15 Okotobala chaka ndi chaka, dziko la Malawi pamodzi ndi dziko lonse limakumbukira mwapadera kufunika kwa mayi ngati nakubala.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open