Wednesday, March 29Malawi's top news source
Shadow

Athana naye Chizuma

Mkulu wa bungwe lolimbana ndi katangale ndi ziphuphu a Martha Chizuma akadali ndi ulendo wautali woteteza ntchito yawo yothana ndi anthu omwe akukhudzidwa ndi nkhani zakatangale komanso ziphuphu m’dziko muno.

Lachitatu lapitali, a Chizuma adalandira kalata kuchokera ku ofesi ya Pulezidenti ndi nduna yosainidwa ndi mlembi wa ofesiyo a Colleen Zamba yowaimitsa ntchito mpaka milandu yomwe akuyankha ithe.

A Zamba ndi a Chizuma pa msonkhano wokambirana zakatangale

Pa tsiku lokumbukira kuthana ndi katangale ndi ziphuphu chaka chatha, a Chizuma adagwedeza dziko atanenetsa pamaso pa mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera ndi nduna zaboma kuti sakuopa kanthu ndipo athana ndi aliyense amene ali m’mafailo awo.

“Ntchito yanga n’kuthana ndi katangale ndi ziphuphu ndiye sindiopa kuti munthu ndiotchuka bwanji, ali ndi ndalama zochuluka bwanji kapena kuti ndi wandale. Ngati mphepo yandipeza kuti adapangapo katangale, akwekwesedwa,” iwo adatero.

Owaimilira pa milandu a Martha Kaukonde adatsimikiza zoti a Chizuma adalandira kalata yowaimitsa ntchito. Koma adati n’zodabwitsa chifukwa adawaimitsa ntchito chifukwa cha mlandu womwe sadapelekere umboni.

“N’zoona awaimitsa, koma n’zodabwitsa chifukwa mlandu omwe akunenawo sitidakalowe [m’khoti] tidzalowa pa 8 February 2023,” adatero a Kaukonde.

Polankhulapo, wapampando wa komiti yoona zamalamulo ku Nyumba ya Malamulo a Peter Dimba adati kuimitsidwa kwa a Chizuma ndinkhani yomvetsa chisoni ndipo yoonekeratu kuti atcheredwa.

“Ndife odabwa komanso okhudzidwa kuti akuluakulu athu akuyesetsa kufuna kukankhira dzikoli kuphedi. Zikutidabwitsa kwambiri komabe izizi zidawonekera patali pomwe,” adatero a Dimba.

Ndipo mkulu wa bungwe la Centre For Democracy and Economic Development Initiative (Cdedi) a Silvestre Namiwa ati akuona kuti chachuluka pankhaniyi n’kufuna kutetezana pakati pa akuluakulu omwe akudziwana kuti adapanga zakatangale.

Kadaulo wa zamalamulo a Garton Kamchedzera adauza The Nation kuti a Chakwera akudzikolakola okha chifukwa adalonjeza pagulu kuti a Chizuma akhalabe mkulu wa ACB

Related News
Malawi Protesters Demand Inquiry Into Allegations Of Rape By Police Officers

EU and Britain ramp up pressure on government to act as street demonstrators converge on Lilongwe Hundreds of rights campaigners Read more

Dust Refusing to Settle for Martha Chizuma

Dust is refusing to settle for Anti-Corruption Bureau (ACB) Director Martha Chizuma as she has been taken to task to Read more

Nancy Tembo clarifies why the president is attending the meeting in America

Minister of Foreign Affairs Nancy Tembo clarifies why the president is attending the meeting in America. She says the president Read more

Malawi president under fire for family appointments to cabinet

New 31-member cabinet includes six figures who are related to each other, although not to the president. Chakwera, 65, comfortably Read more

Zameer Karim accused of intent to defraud Ecobank

Businessman Zameer Karim is facing a charge of intent to defraud Ecobank over K850 million, which is connected to Police Read more

MWENYE KIDNAPPING SAGA: Mustak Chotia implicates Mr Dipak Jevant of Sealand Investments

Mr Mustak Chotia, the mafia who masterminded the kidnapping of Shayona Cement Managing Director has implicated Mr Dipak Jevant, Managing Read more

Malawi Police zero on Indian Community’s kidnapper ring leader: Lebanese lady Rola Nasr Eldinne involved

Kadadzera: We are still investigating The issue of kidnapping and attempts on Indian community in Malawi with evil intentions is Read more

Fear grips Malawi’s Asian community over attacks, kidnapping

                                        Read more

Mustaq Chotia Implicates Mr Dipak Jevant mastermind kidnapping Shayona Boss

Mr Mustak Chotia, the mafia who masterminded the kidnapping of Shayona Cement official has implicated Mr Dipak Jevant, Managing Director Read more

Oops! Batatawala’s Son On the Loose

The Anti Corruption Bureau ( ACB ) has arrested self styled Blantyre businessperson Lido Karim also known as Batatawala two Read more

News To Read

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *