Fri. Apr 19th, 2024

Athana naye Chizuma

Mkulu wa bungwe lolimbana ndi katangale ndi ziphuphu a Martha Chizuma akadali ndi ulendo wautali woteteza ntchito yawo yothana ndi anthu omwe akukhudzidwa ndi nkhani zakatangale komanso ziphuphu m’dziko muno.

Lachitatu lapitali, a Chizuma adalandira kalata kuchokera ku ofesi ya Pulezidenti ndi nduna yosainidwa ndi mlembi wa ofesiyo a Colleen Zamba yowaimitsa ntchito mpaka milandu yomwe akuyankha ithe.

A Zamba ndi a Chizuma pa msonkhano wokambirana zakatangale

Pa tsiku lokumbukira kuthana ndi katangale ndi ziphuphu chaka chatha, a Chizuma adagwedeza dziko atanenetsa pamaso pa mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera ndi nduna zaboma kuti sakuopa kanthu ndipo athana ndi aliyense amene ali m’mafailo awo.

“Ntchito yanga n’kuthana ndi katangale ndi ziphuphu ndiye sindiopa kuti munthu ndiotchuka bwanji, ali ndi ndalama zochuluka bwanji kapena kuti ndi wandale. Ngati mphepo yandipeza kuti adapangapo katangale, akwekwesedwa,” iwo adatero.

Owaimilira pa milandu a Martha Kaukonde adatsimikiza zoti a Chizuma adalandira kalata yowaimitsa ntchito. Koma adati n’zodabwitsa chifukwa adawaimitsa ntchito chifukwa cha mlandu womwe sadapelekere umboni.

“N’zoona awaimitsa, koma n’zodabwitsa chifukwa mlandu omwe akunenawo sitidakalowe [m’khoti] tidzalowa pa 8 February 2023,” adatero a Kaukonde.

Polankhulapo, wapampando wa komiti yoona zamalamulo ku Nyumba ya Malamulo a Peter Dimba adati kuimitsidwa kwa a Chizuma ndinkhani yomvetsa chisoni ndipo yoonekeratu kuti atcheredwa.

“Ndife odabwa komanso okhudzidwa kuti akuluakulu athu akuyesetsa kufuna kukankhira dzikoli kuphedi. Zikutidabwitsa kwambiri komabe izizi zidawonekera patali pomwe,” adatero a Dimba.

Ndipo mkulu wa bungwe la Centre For Democracy and Economic Development Initiative (Cdedi) a Silvestre Namiwa ati akuona kuti chachuluka pankhaniyi n’kufuna kutetezana pakati pa akuluakulu omwe akudziwana kuti adapanga zakatangale.

Kadaulo wa zamalamulo a Garton Kamchedzera adauza The Nation kuti a Chakwera akudzikolakola okha chifukwa adalonjeza pagulu kuti a Chizuma akhalabe mkulu wa ACB

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

President Lazarus Chakwera has officially opened the Blantyre International Cancer Centre, The private health facility, has been constructed by the Thomson and Barbara Mpinganjira Foundation