Friday, March 29
Shadow

Chipani Cha DPP Agwirizana Kuti Nankhumwa akhalebe pampandowu.

Kusamvana komwe kunalipo m’chipani cha DPP pa yemwe akuyenera kukhala mkulu wa zipani zotsuta boma m’nyumba ya malamulo kwatha tsopano.

Izi zikutsatira m’gwirizano omwe mbali zokhuzidwa zapanga kuti a Kondwani Nankhumwa akhalebe pampandowu.

Malingana ndi mneneri wa chipani cha DPP, Shadrec Namalomba, a Nankhumwa akhalabe pa udindowu kufikira pomwe chipanichi chidzachititsenso chisankho china cha mtsogoleri wa zipani zotsutsa m’nyumbayi.

“Tinafunsa bwalo la milandu kuti litipatse nthawi yomwe tingakhale titachitanso chisankhochi, koma wodandawula anakana kuti izi zisakhudzee bwalo la milandu,” yatero kalata yomwe a Namalomba atulutsa.

Ganizoli ladza kutsatira zokambirana zomwe zachitika ndipo mkhala pakati wake anali oweluza milandu, Kenyatta Nyirenda.

Kusamvanaku kunadza, pomwe aphungu ena a DPP anasankha a George Chaponda kukhala pa udindowu pa mkumano wawo wina ku nyumba ya mtsogoleri wa chipanichi, Peter Mutharika ku Mangochi.

Aphungu ena sadakondwe ndi izi ndipo anakamang’ala ku bwalo la milandu.

Mbali ya a Chaponda akuti yavomerezanso kuti inalakwitsa kuwasankha pa mpandowu popanda aphungu ena.

Related Posts

DPP Blues Rebels Brings Division In

DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

President Lazarus Chakwera has officially opened the Blantyre International Cancer Centre, The private health facility, has been constructed by the Thomson and Barbara Mpinganjira Foundation