Kusamvana komwe kunalipo m’chipani cha DPP pa yemwe akuyenera kukhala mkulu wa zipani zotsuta boma m’nyumba ya malamulo kwatha tsopano.
Izi zikutsatira m’gwirizano omwe mbali zokhuzidwa zapanga kuti a Kondwani Nankhumwa akhalebe pampandowu.
Malingana ndi mneneri wa chipani cha DPP, Shadrec Namalomba, a Nankhumwa akhalabe pa udindowu kufikira pomwe chipanichi chidzachititsenso chisankho china cha mtsogoleri wa zipani zotsutsa m’nyumbayi.
“Tinafunsa bwalo la milandu kuti litipatse nthawi yomwe tingakhale titachitanso chisankhochi, koma wodandawula anakana kuti izi zisakhudzee bwalo la milandu,” yatero kalata yomwe a Namalomba atulutsa.
Read also: Malawi And Failed Leadership
Read also: Opposition Parties Demand Immediate Action from MEC Chairperson Anabel Mtalimanja
Read also: THE PUBLIC-PRIVATE PARTNERSHIP BILL: A LICENCE TO STEAL-BRIGHT MSAKA
Ganizoli ladza kutsatira zokambirana zomwe zachitika ndipo mkhala pakati wake anali oweluza milandu, Kenyatta Nyirenda.
Kusamvanaku kunadza, pomwe aphungu ena a DPP anasankha a George Chaponda kukhala pa udindowu pa mkumano wawo wina ku nyumba ya mtsogoleri wa chipanichi, Peter Mutharika ku Mangochi.
Aphungu ena sadakondwe ndi izi ndipo anakamang’ala ku bwalo la milandu.
Mbali ya a Chaponda akuti yavomerezanso kuti inalakwitsa kuwasankha pa mpandowu popanda aphungu ena.
Read also: Minister Gives Contractor Ultimatum
Read also: Betrayal Through Silence: When Power Forgets Its Fighters, Collapse Begins-Jumbe
Read also: MERA Sensitises Stakeholders on Revised Standards for Construction of Fuel Service Stations





